Masalimo 75 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 75:1-10

Salimo 75

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo.

1Tikuthokoza Inu Mulungu,

tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe,

anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.

2Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera,

ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.

3Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera,

ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba.

Sela

4Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’

ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.

5Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba;

musayankhule ndi khosi losololoka.’ ”

6Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo

kapena ku chipululu.

7Koma ndi Mulungu amene amaweruza:

Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.

8Mʼdzanja la Yehova muli chikho

chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera;

Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi

amamwa ndi senga zake zonse.

9Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya;

ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.

10Ndidzadula nyanga za onse oyipa

koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 75:1-11

Guds retfærdige dom

1Til korlederen: En lovsang af Asaf.

2Vi priser og takker dig, Gud,

vi glæder os over din godhed.

Du er os altid nær,

og vi oplever din underfulde hjælp.

3Dommen kommer til den fastsatte tid,

og det bliver en retfærdig dom.

4Jorden skal ryste og menneskene skælve,

men Gud står urokkeligt fast.

5Jeg siger til de stolte: „Vær ikke hovmodige.”

Jeg advarer de gudløse: „Vær ikke selvsikre.

6Prøv ikke på at kæmpe mod himlens Gud,

sæt jer endelig ikke op imod ham.

7Dommen kommer hverken fra øst eller vest,

eller fra ørkenen nede mod syd.

8For det er Gud, der dømmer os alle:

han ydmyger den ene og ophøjer den anden.

9Herren holder et bæger i hånden,

hans vrede bobler som en krydret vin.

Han udøser sin straf over alle de onde,

de skal tømme bægeret til sidste dråbe.”

10Men jeg vil altid juble og glædes,

takke og lovprise Israels Gud,

11for han vil bryde de gudløses magt,

men de gudfrygtiges styrke skal vokse.