Masalimo 74 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 74:1-23

Salimo 74

Ndakatulo ya Asafu.

1Nʼchifukwa chiyani mwatitaya ife kwamuyaya, Inu Mulungu?

Chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukutukutira pa nkhosa za busa lanu?

2Kumbukirani anthu amene munawagula kalekale,

fuko la cholowa chanu, limene Inu munaliwombola,

phiri la Ziyoni, kumene inuyo mumakhala.

3Tembenuzani mapazi kuloza ku mabwinja awa amuyaya

chiwonongeko ichi chonse mdani wabweretsa pa malo opatulika.

4Adani anu anabangula pa malo pamene Inu munkakumana nafe;

anayimika mbendera zawo monga zizindikiro zachigonjetso.

5Iwo anachita ngati anthu oti anyamula mbendera zawo

kuti adule mitengo mʼnkhalango.

6Kenaka anaphwanya ndi nkhwangwa ndi akasemasema awo

zonse zimene tinapachika.

7Iwo anatentha malo anu opatulika mpaka kuwagwetsa pansi;

anadetsa malo okhalamo dzina lanu.

8Ndipo anati mʼmitima yawo, “Tawatha kwathunthu.”

Anatentha malo aliwonse amene Mulungu amapembedzedwerako mʼdzikomo.

9Ife sitinapatsidwe chizindikiro chodabwitsa;

palibe aneneri amene atsala

ndipo palibe aliyense wa ife akudziwa kuti izi zidzatenga nthawi yayitali bwanji.

10Kodi mpaka liti, mdani adzanyoze Inu Mulungu?

Kodi amaliwongowa adzapeputsa dzina lanu kwamuyaya?

11Chifukwa chiyani mukubweza dzanja lanu lamanja?

Litulutseni kuchoka pachifuwa chanu ndipo muwawononge!

12Koma Inu Mulungu, ndinu Mfumu yanga kuyambira kalekale;

Mumabweretsa chipulumutso pa dziko lapansi.

13Ndinu amene munagawa nyanja ndi mphamvu yanu;

munathyola mitu ya zirombo za mʼmadzi.

14Ndinu amene munaphwanya mitu ya Leviyatani

ndi kuyipereka ngati chakudya cha zirombo za mʼchipululu.

15Ndinu amene munatsekula akasupe ndi mitsinje,

munawumitsa mitsinje imene siphwa nthawi zonse.

16Masana ndi anu ndipo usiku ndi wanunso;

Inuyo munakhazikitsa dzuwa ndi mwezi.

17Ndinu amene munakhazikitsa malire onse a dziko lapansi;

munakhazikitsa chilimwe ndi dzinja.

18Kumbukirani momwe mdani wakunyozerani Inu Yehova,

momwe anthu opusa apeputsira dzina lanu.

19Musapereke moyo wa nkhunda yanu ku zirombo zakuthengo;

nthawi zonse musayiwale miyoyo ya anthu anu osautsidwa.

20Mukumbukire pangano lanu, pakuti malo obisika a mʼdziko

asanduka mochitira zachiwawa zochuluka.

21Musalole kuti osautsidwa abwerere mwamanyazi;

osauka ndi osowa atamande dzina lanu.

22Dzukani Inu Mulungu ndipo dzitetezeni pa mlandu;

kumbukirani momwe opusa akukunyozerani tsiku lonse.

23Musalekerere phokoso la otsutsana nanu,

chiwawa cha adani anu, chimene chikumveka kosalekeza.

Hoffnung für Alle

Psalm 74:1-23

Gottes Tempel – ein Trümmerhaufen!

1Von Asaf, zum Nachdenken.

Gott, warum hast du uns für immer verstoßen?

Warum lässt du deinen Zorn an uns aus?

Wir gehören doch zu dir wie Schafe zu ihrem Hirten!

2Erinnere dich daran, dass wir dein Volk sind!

Vor langer Zeit hast du uns angenommen

und uns aus der Gefangenschaft befreit. Wir alle sind dein Eigentum!

Denke an den Berg Zion, den du dir als Wohnsitz erwählt hast!

3Geh über die Trümmer, die schon so lange dort liegen;

sieh doch: Alles haben die Feinde im Heiligtum verwüstet!

4Ihr Triumphgeschrei entweihte die Stätte, wo du uns begegnet bist,

ihre Fahnen haben sie als Zeichen des Sieges gehisst.

5In deinem Tempel sieht es so aus,

als hätte man darin Kleinholz gehackt:

6Die kostbaren Schnitzereien haben sie

mit Äxten und Brechstangen zertrümmert.

7Danach steckten sie dein Heiligtum in Brand,

sie entweihten den Ort, wo du angebetet wurdest.

8Sie hatten vor, uns alle vernichtend zu schlagen,

im ganzen Land brannten sie die heiligen Stätten nieder.

9Nichts mehr deutet darauf hin, dass du noch Herr der Lage bist.74,9 Wörtlich: Zeichen für uns sehen wir nicht.

Es gibt keinen Propheten mehr –

niemand von uns weiß, wie lange das noch so weitergehen soll.

10Wie lange, Gott, willst du es dir gefallen lassen,

dass die Feinde dich schamlos verhöhnen?

Sollen sie für immer deinen Namen in den Schmutz ziehen?

11Warum hältst du dich zurück? Warum greifst du nicht ein?

Zeige deine Macht und vernichte sie!

12Gott, seit uralter Zeit bist du unser König74,12 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text lautet: mein König.,

schon oft hast du unser Land gerettet.

13Du hast mit deiner Macht das Meer gespalten

und den Seedrachen die Schädel zerschmettert.

14Ja, du hast dem Seeungeheuer74,14 Wörtlich: dem Leviatan. die Köpfe abgehauen

und es den Wüstentieren zum Fraß vorgeworfen.

15Du ließest Quellen und Bäche hervorsprudeln

und brachtest große Ströme zum Versiegen.

16Dir gehört der Tag und auch die Nacht,

du hast die Sonne und den Mond geschaffen.

17Du hast alle Grenzen der Erde festgelegt,

hast Sommer und Winter gemacht.

18Höre doch, Herr, wie deine Feinde dich verhöhnen!

Dieses gewissenlose Volk zieht deinen Namen in den Schmutz!

19Liefere uns nicht diesen Raubtieren aus,

du weißt doch, wie hilflos wir sind!74,19 Wörtlich: Gib das Leben deiner Taube nicht den Tieren preis.

Sieh unserem Leid nicht länger tatenlos zu,

20sondern denke an deinen Bund mit uns!

Selbst in den Schlupfwinkeln des Landes

ist niemand mehr vor roher Gewalt sicher.

21Herr, wir werden schwer bedrängt,

lass uns nicht in Schimpf und Schande enden!

Ohne dich sind wir arm und wehrlos –

rette uns, damit wir dich loben können!

22Gott, greife endlich ein, denn ihr Angriff gilt dir!

Sorge dafür, dass du recht behältst!

Sieh auf diese Meute, die dich Tag für Tag verspottet!

23Ständig lärmen deine Feinde und lehnen sich gegen dich auf.

Vergiss ihre Schmähungen nicht!