Salimo 70
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho.
1Fulumirani Mulungu kundipulumutsa;
Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
2Iwo amene akufunafuna moyo wanga
achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;
onse amene akukhumba chiwonongeko changa
abwezedwe mopanda ulemu.
3Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,”
abwerere chifukwa cha manyazi awo.
4Koma onse amene akufunafuna Inu
akondwere ndi kusangalala mwa Inu;
iwo amene amakonda chipulumutso chanu
nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
5Koma ine ndine wosauka ndi wosowa;
bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu.
Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga;
Inu Yehova musachedwe.
Psalm 70In Hebrew texts 70:1-5 is numbered 70:2-6.
For the director of music. Of David. A petition.
1Hasten, O God, to save me;
come quickly, Lord, to help me.
2May those who want to take my life
be put to shame and confusion;
may all who desire my ruin
be turned back in disgrace.
3May those who say to me, ‘Aha! Aha!’
turn back because of their shame.
4But may all who seek you
rejoice and be glad in you;
may those who long for your saving help always say,
‘The Lord is great!’
5But as for me, I am poor and needy;
come quickly to me, O God.
You are my help and my deliverer;
Lord, do not delay.