Masalimo 68 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 68:1-35

Salimo 68

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane;

adani ake athawe pamaso pake.

2Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali.

Monga phula limasungunukira pa moto,

oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.

3Koma olungama asangalale

ndi kukondwera pamaso pa Mulungu;

iwo akondwere ndi kusangalala.

4Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando,

mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo;

dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.

5Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye,

ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.

6Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja,

amatsogolera amʼndende ndi kuyimba;

koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.

7Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu,

pamene munayenda kudutsa chipululu,

8dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula,

pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai.

Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.

9Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu;

munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.

10Anthu anu anakhala mʼmenemo

ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.

11Ambuye analengeza mawu,

ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;

12“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro;

mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.

13Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto,

mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva,

nthenga zake ndi golide wonyezimira.”

14Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko,

zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.

15Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero;

mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.

16Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri,

pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira,

kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?

17Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka,

ndi miyandamiyanda;

Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.

18Pamene Inu munakwera mmwamba,

munatsogolera a mʼndende ambiri;

munalandira mphatso kuchokera kwa anthu,

ngakhale kuchokera kwa owukira,

kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.

19Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu

amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.

20Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa;

Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.

21Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake,

zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.

22Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani;

ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.

23Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu,

pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”

24Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu;

mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.

25Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo;

pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.

26Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu;

tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.

27Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera,

pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda,

ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.

28Kungani mphamvu zanu Mulungu;

tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.

29Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu,

mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.

30Dzudzulani chirombo pakati pa mabango,

gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu.

Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva.

Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.

31Nthumwi zidzachokera ku Igupto;

Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.

32Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi

imbirani Ambuye matamando.

Sela

33Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba

amene amabangula ndi mawu amphamvu.

34Lengezani za mphamvu za Mulungu,

amene ulemerero wake uli pa Israeli

amene mphamvu zake zili mʼmitambo.

35Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika;

Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake.

Matamando akhale kwa Mulungu!

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 68:1-35

Salmo 68

Al director musical. Salmo de David. Cántico.

1Que se levante Dios,

que sean dispersados sus enemigos,

que huyan de su presencia los que le odian.

2Que desaparezcan del todo,

como humo que se disipa con el viento;

que perezcan ante Dios los impíos,

como cera que se derrite en el fuego.

3Pero que los justos se alegren y se regocijen;

que estén felices y alegres delante de Dios.

4Cantad a Dios, cantad salmos a su nombre;

aclamad a quien cabalga por las estepas,

y regocijaos en su presencia.

¡Su nombre es el Señor!

5Padre de los huérfanos y defensor de las viudas

es Dios en su morada santa.

6Dios da un hogar a los desamparados

y libertad a los cautivos;

los rebeldes habitarán en el desierto.

7Cuando saliste, oh Dios, al frente de tu pueblo,

cuando a través de los páramos marchaste, Selah

8la tierra se estremeció,

los cielos se vaciaron,

delante de Dios, el Dios de Sinaí,

delante de Dios, el Dios de Israel.

9Tú, oh Dios, diste abundantes lluvias;

reanimaste a tu extenuada herencia.

10Tu familia se estableció en la tierra

que en tu bondad, oh Dios, preparaste para el pobre.

11El Señor ha emitido la palabra,

y millares de mensajeras la proclaman:

12«Van huyendo los reyes y sus tropas;

en las casas, las mujeres se reparten el botín:

13alas de paloma cubiertas de plata,

con plumas de oro resplandeciente.

Tú te quedaste a dormir entre los rebaños».

14Cuando el Todopoderoso puso en fuga

a los reyes de la tierra,

parecían copos de nieve

cayendo sobre la cumbre del Zalmón.

15Montañas de Basán, montañas imponentes;

montañas de Basán, montañas escarpadas:

16¿Por qué, montañas escarpadas, miráis con envidia

al monte donde a Dios le place residir,

donde el Señor habitará por siempre?

17Los carros de guerra de Dios

se cuentan por millares;

del Sinaí vino en ellos el Señor

para entrar en su santuario.

18Cuando tú, Dios y Señor,

ascendiste a las alturas,

te llevaste contigo a los cautivos;

tomaste tributo de los hombres,

aun de los rebeldes,

para establecer tu morada.

19Bendito sea el Señor, nuestro Dios y Salvador,

que día tras día sobrelleva nuestras cargas. Selah

20Nuestro Dios es un Dios que salva;

el Señor Soberano nos libra de la muerte.

21Dios aplastará la cabeza de sus enemigos,

la testa enmarañada de los que viven pecando.

22El Señor nos dice: «De Basán los haré regresar;

de las profundidades del mar los haré volver,

23para que se empapen los pies

en la sangre de sus enemigos;

para que, al lamerla, los perros

tengan también su parte».

24En el santuario pueden verse

el cortejo de mi Dios,

el cortejo de mi Dios y Rey.

25Los cantores van al frente,

seguidos de los músicos de cuerda,

entre doncellas que tocan panderetas.

26Bendecid a Dios en la gran congregación;

alabad al Señor, descendientes de Israel.

27Los guía la joven tribu de Benjamín,

seguida de los múltiples príncipes de Judá

y de los príncipes de Zabulón y Neftalí.

28Despliega tu poder, oh Dios;

haz gala, oh Dios, de tu poder,

que has manifestado en favor nuestro.

29A causa de tu templo en Jerusalén

los reyes te ofrecerán presentes.

30Reprende a esa bestia de los juncos,

a esa manada de toros bravos

entre naciones que parecen becerros.

Haz que, humillada, te lleve lingotes de plata;

dispersa a las naciones belicosas.

31Egipto enviará embajadores,

y Cus se someterá a Dios.

32Cantad a Dios, oh reinos de la tierra,

cantad salmos al Señor, Selah

33al que cabalga por los cielos,

los cielos antiguos,

al que hace oír su voz,

su voz de trueno.

34Reconoced el poder de Dios;

su majestad está sobre Israel,

su poder está en las alturas.

35En tu santuario, oh Dios, eres imponente;

¡el Dios de Israel da poder y fuerza a su pueblo!

¡Bendito sea Dios!