Masalimo 64 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 64:1-10

Salimo 64

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;

tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.

2Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,

ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.

3Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,

amaponya mawu awo olasa ngati mivi.

4Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;

amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.

5Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,

amayankhula zobisa misampha yawo;

ndipo amati, “Adzayiona ndani?”

6Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,

“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”

Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.

7Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;

mwadzidzidzi adzakanthidwa.

8Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa

ndi kuwasandutsa bwinja;

onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.

9Anthu onse adzachita mantha;

adzalengeza ntchito za Mulungu

ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.

10Lolani wolungama akondwere mwa Yehova

ndi kubisala mwa Iye,

owongoka mtima onse atamande Iye!

New International Reader’s Version

Psalm 64:1-10

Psalm 64

For the director of music. A psalm of David.

1God, hear me as I tell you my problem.

Don’t let my enemies kill me.

2Hide me from evil people who talk about how to harm me.

Hide me from those people who are planning to do evil.

3They make their tongues like sharp swords.

They aim their mean words like deadly arrows.

4They shoot from their hiding places at people who aren’t guilty.

They shoot quickly and aren’t afraid of being caught.

5They help one another make evil plans.

They talk about hiding their traps.

They say, “Who can see what we are doing?”

6They make plans to do what is evil.

They say, “We have thought up a perfect plan!”

The hearts and minds of people are so clever!

7But God will shoot my enemies with his arrows.

He will suddenly strike them down.

8He will turn their own words against them.

He will destroy them.

All those who see them will shake their heads

and look down on them.

9All people will respect God.

They will tell about his works.

They will think about what he has done.

10Godly people will be full of joy because of what the Lord has done.

They will go to him for safety.

All those whose hearts are honest will be proud of what he has done.