Masalimo 64 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 64:1-10

Salimo 64

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga;

tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.

2Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa,

ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.

3Iwo amanola malilime awo ngati malupanga,

amaponya mawu awo olasa ngati mivi.

4Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa;

amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.

5Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa,

amayankhula zobisa misampha yawo;

ndipo amati, “Adzayiona ndani?”

6Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati,

“Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!”

Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.

7Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi;

mwadzidzidzi adzakanthidwa.

8Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa

ndi kuwasandutsa bwinja;

onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.

9Anthu onse adzachita mantha;

adzalengeza ntchito za Mulungu

ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.

10Lolani wolungama akondwere mwa Yehova

ndi kubisala mwa Iye,

owongoka mtima onse atamande Iye!

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 64:1-10

第 64 篇

祈求上帝的保護

大衛作的詩,交給樂長。

1上帝啊,求你傾聽我的苦訴,

求你保護我的性命不受仇敵的威脅。

2求你保護我免遭惡人的謀害,

使我脫離不法之徒。

3他們舌頭鋒利如刀,

言語惡毒如箭穿心。

4他們埋伏起來,

暗箭傷害純全無過的人。

他們突然襲擊,毫無顧忌。

5他們狼狽為奸,

商量暗設網羅,

以為誰也看不見。

6他們圖謀不義之事,

認為策劃得無懈可擊。

人心真是狡猾。

7但上帝必用箭射他們,

將他們突然射倒在地。

8他們必自作自受,

被自己的舌頭所害。

看見的人都嘲笑他們。

9這樣,人人必敬畏上帝,

傳揚祂奇妙的作為,

思想祂所做的事。

10義人必因耶和華而歡欣,

並且投靠祂,

心地正直的人必讚美祂。