Masalimo 63 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 63:1-11

Salimo 63

Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda.

1Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga,

moona mtima ine ndimakufunafunani;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu,

thupi langa likulakalaka inu,

mʼdziko lowuma ndi lotopetsa

kumene kulibe madzi.

2Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika

ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.

3Chifukwa chikondi chanu

ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.

4Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga,

ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.

5Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona.

Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.

6Pa bedi panga ndimakumbukira inu;

ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.

7Chifukwa ndinu thandizo langa,

ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.

8Moyo wanga umakangamira Inu;

dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.

9Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa;

adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.

10Iwo adzaperekedwa ku lupanga

ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.

11Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;

onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo,

koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 63:1-11

Salmo 63

Salmo de David, cuando estaba en el desierto de Judá.

1Oh Dios, tú eres mi Dios;

yo te busco intensamente.

Mi alma tiene sed de ti;

todo mi ser te anhela,

cual tierra seca, extenuada y sedienta.

2Te he visto en el santuario

y he contemplado tu poder y tu gloria.

3Tu amor es mejor que la vida;

por eso mis labios te alabarán.

4Te bendeciré mientras viva,

y alzando mis manos te invocaré.

5Mi alma quedará satisfecha

como de un suculento banquete,

y con labios jubilosos

te alabará mi boca.

6En mi lecho me acuerdo de ti;

pienso en ti toda la noche.

7A la sombra de tus alas cantaré,

porque tú eres mi ayuda.

8Mi alma se aferra a ti;

tu mano derecha me sostiene.

9Los que buscan mi muerte serán destruidos;

bajarán a las profundidades de la tierra.

10Serán entregados a la espada

y acabarán devorados por los chacales.

11El rey se regocijará en Dios;

todos los que invocan a Dios lo alabarán,

pero los mentirosos serán silenciados.