Masalimo 62 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 62:1-12

Salimo 62

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.

1Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;

chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.

2Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.

3Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?

Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,

ngati mpanda wogwedezeka?

4Iwo akufunitsitsa kumugwetsa

kuti achoke pa malo ake apamwamba.

Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.

Ndi pakamwa pawo amadalitsa

koma mʼmitima yawo amatemberera.

5Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;

chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.

6Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.

7Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:

Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.

8Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;

khuthulani mitima yanu kwa Iye,

pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.

Sela

9Anthu wamba ndi mpweya chabe;

anthu apamwamba ndi bodza chabe;

ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;

iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe

10Musadalire kulanda mwachinyengo

kapena katundu wobedwa;

ngakhale chuma chanu chichuluke,

musayike mtima wanu pa icho.

11Mulungu wayankhula kamodzi,

ine ndamvapo zinthu ziwiri;

choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,

12komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.

Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu

molingana ndi ntchito zake.

Священное Писание

Забур 62:1-12

Песнь 62

1Песнь Давуда, когда он был в Иудейской пустыне62:1 См. 1 Цар. 23–24; 2 Цар. 15:13–17:29..

2Всевышний, Ты – мой Бог!

Тебя с ранней зари я ищу.

Душа моя жаждет Тебя,

тело моё по Тебе томится

в краю сухом и бесплодном,

где нет воды.

3Я смотрел на Тебя в святилище

и видел силу Твою и славу.

4Уста мои будут славить Тебя,

потому что Твоя милость лучше жизни.

5Прославлю Тебя, пока я жив,

и руки во имя Твоё вознесу.

6Словно лучшими яствами душа моя насыщается,

и уста Тебя славят радостно,

7когда вспоминаю Тебя на ложе своём

и думаю в час ночной о Тебе,

8потому что Ты – моя помощь,

и в тени Твоих крыльев я возрадуюсь.

9Душа моя льнёт к тебе;

Ты правой рукой поддерживаешь меня.

10Те, кто желает моей смерти,

сойдут в нижний мир.

11От меча падут они,

став добычей шакалов.

12Царь же возликует о Всевышнем,

и все, кто клянётся Всевышним, восхвалят Его,

а уста лжецов умолкнут.