Masalimo 6 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 6:1-10

Salimo 6

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide.

1Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu,

kapena kundilanga mu ukali wanu.

2Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka;

Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.

3Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu.

Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?

4Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse;

pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

5Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira;

Amakutamandani ndani ali ku manda?

6Ine ndatopa ndi kubuwula;

usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga;

ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.

7Maso anga atupa chifukwa cha chisoni;

akulephera kuona chifukwa cha adani anga.

8Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa,

pakuti Yehova wamva kulira kwanga.

9Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo;

Yehova walandira pemphero langa.

10Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha;

adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

Hoffnung für Alle

Psalm 6:1-11

Herr, strafe mich nicht länger!

1Ein Lied von David, mit einem tief gestimmten6,1 Oder: achtsaitigen. – Das hebräische Wort ist nicht sicher zu deuten. So auch in Psalm 12,1. Saiteninstrument zu begleiten.

2Herr, du lässt mich deinen Zorn spüren.

Ich flehe dich an: Strafe mich nicht länger!

3Hab Erbarmen mit mir, Herr, ich sieche dahin!

Heile mich, denn ich bin am Ende meiner Kraft!

4Ich weiß weder aus noch ein.

Herr, wie lange willst du dir das noch ansehen?

5Wende dich mir wieder zu, Herr, und rette mich!

Hilf mir, du bist doch ein barmherziger Gott!

6Wenn ich tot bin, kann ich dir nicht mehr danken.

Wie soll ich dich denn im Totenreich loben?

7-8Ach, ich bin müde vom Stöhnen.

Nachts im Bett weine ich, bis die Kissen durchnässt

und meine Augen ganz verquollen sind.

Daran sind nur meine Feinde schuld,

sie haben mich in die Enge getrieben.

9Ihr Verbrecher, verschwindet,

denn der Herr hat meine Tränen gesehen!

10Ja, der Herr hat mein Schreien gehört,

er nimmt mein Gebet an.

11Meine Feinde aber werden zu Tode erschrecken,

sie werden mit Schimpf und Schande überhäuft.

Ehe sie damit rechnen, müssen sie die Flucht ergreifen!