Masalimo 57 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 57:1-11

Salimo 57

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga.

1Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo,

pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo.

Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu

mpaka chiwonongeko chitapita.

2Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba,

kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.

3Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa,

kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri.

Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.

4Ine ndili pakati pa mikango,

ndagona pakati pa zirombo zolusa;

anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi,

malilime awo ndi malupanga akuthwa.

5Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba;

mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

6Iwo anatchera mapazi anga ukonde

ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa.

Anakumba dzenje mʼnjira yanga

koma agweramo okha mʼmenemo.

7Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu

mtima wanga ndi wokhazikika.

Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.

8Dzuka moyo wanga!

Dzukani zeze ndi pangwe!

Ndidzadzuka mʼbandakucha.

9Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu,

ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.

10Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba;

kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.

11Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba,

mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 57:1-11

第 57 篇

被圍困中的呼求

大衛作的詩,交給樂長,調用「休要毀壞」。當時他因逃避掃羅躲進了洞裡。

1上帝啊,求你憐憫我,憐憫我,

因為我投靠你。

我要在你翅膀下得到蔭庇,

直到災難結束。

2我向至高的上帝,

向為我成就一切的上帝呼求。

3上帝從天上施助、拯救我,

使迫害我的人蒙羞。

上帝必彰顯祂的慈愛和信實。

4我被獅子包圍,

躺臥在吃人的野獸中。

他們的牙齒是矛和箭,

舌頭是尖刀。

5上帝啊,

願人對你的尊崇超過諸天,

願你的榮耀覆蓋大地。

6我的仇敵設下網羅,

我心中沮喪。

他們在我走的路上挖了陷阱,

自己卻掉了進去。(細拉)

7上帝啊,我心堅定,我心堅定,

我要唱詩讚美你。

8我的心啊,要振奮起來!

琴瑟啊,彈奏吧!

我要喚醒黎明!

9主啊,我要在列邦稱謝你,

在列國歌頌你。

10因為你的慈愛高達諸天,

你的信實廣及穹蒼。

11上帝啊,

願你得到的尊崇超過諸天,

願你的榮耀覆蓋大地。