Masalimo 56 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 56:1-13

Salimo 56

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati.

1Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri;

tsiku lonse akundithira nkhondo.

2Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse,

ambiri akumenyana nane monyada.

3Ndikachita mantha

ndimadalira Inu.

4Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,

mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.

Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?

5Tsiku lonse amatembenuza mawu anga;

nthawi zonse amakonza zondivulaza.

6Iwo amakambirana, amandibisalira,

amayangʼanitsitsa mayendedwe anga

ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.

7Musalole konse kuti athawe;

mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.

8Mulembe za kulira kwanga,

mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu.

Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?

9Adani anga adzabwerera mʼmbuyo

pamene ndidzalirira kwa Inu.

Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.

10Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda,

mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,

11mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha.

Kodi munthu angandichite chiyani?

12Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu;

ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.

13Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa

ndi mapazi anga kuti ndingagwe,

kuti ndiyende pamaso pa Mulungu

mʼkuwala kwa moyo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Забур 56:1-12

Песнь 56

(Заб. 107:2-6)

1Дирижёру хора. На мотив «Не погуби»56:1 Не погуби – вероятно, зачин, начальные слова текста или названия песни (возможно, на основании Ис. 65:8). Возможно, такое замечание запрещало удалять заголовок или сам текст песни. То же в песнях 57, 58 и 74.. Мольба Довуда, когда он убежал от Шаула в пещеру56:1 См. 1 Цар. 22:1-2; 24:1-23..

2Всевышний, помилуй меня, помилуй!

У Тебя я ищу прибежища.

Я укроюсь в тени Твоих крыльев,

пока не пройдёт беда.

3Я взываю к Богу Высочайшему,

к Всевышнему, вершащему замысел Свой обо мне.

4Он пошлёт помощь с небес и спасёт меня,

посрамит гонителя моего; Пауза

пошлёт Всевышний милость Свою и верность.

5Львы меня окружили,

я лежу среди хищных зверей –

средь людей, чьи зубы – копья и стрелы,

чьи языки – наточенные мечи.

6Выше небес будь превознесён, о Всевышний;

над всей землёй да будет слава Твоя!

7Для ног моих они сеть раскинули;

сникла от горя моя душа.

На пути моём они вырыли яму,

но сами в неё упали. Пауза

8Сердце моё твёрдо, Всевышний, сердце моё твёрдо.

Буду петь и славить Тебя.

9Пробудись, моя душа!

Пробудитесь, лира и арфа!

Я проснусь на заре.

10Восхвалю Тебя, Владыка, среди народов,

воспою Тебя среди племён,

11потому что милость Твоя велика, до самых небес,

и верность Твоя достигает облаков.

12Выше небес будь превознесён, о Всевышний;

над всей землёй да будет слава Твоя!