Masalimo 54 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 54:1-7

Salimo 54

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

1Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;

onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.

2Imvani pemphero langa, Inu Mulungu

mvetserani mawu a pakamwa panga.

3Alendo akundithira nkhondo;

anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,

anthu amene salabadira za Mulungu.

4Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;

Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

5Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;

mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

6Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;

ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,

pakuti ndi labwino.

7Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,

ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 54:1-9

Bøn om hjælp mod fjenden

1-2Til korlederen: En visdomssang af David, dengang folkene fra Zif kom og fortalte Saul, at David skjulte sig hos dem. Synges til akkompagnement af strengeinstrumenter.

3Kom mig til hjælp, almægtige Gud,

jeg ved, du har magt til at redde mig.

4Hør min bøn, oh, Gud,

og lyt til mine ord.

5Fremmede folkeslag rejser sig imod mig,

voldsmænd vil mig til livs,

de regner slet ikke med dig.

6Men du er min redning, Gud,

du er den, der holder mig i live.

7Lad fjenderne blive straffet for deres ondskab.

Gør det af med dem, Herre,

for du er trofast imod mig.

8Så vil jeg ofre til dig med glæde,

jeg vil lovprise dig, Gud, for du er god.

9Du udfrier mig fra alle mine problemer,

og jeg ser mine fjender blive besejret.