Masalimo 5 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 5:1-12

Salimo 5

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe zoyimbira za zitoliro. Salimo la Davide.

1Tcherani khutu ku mawu anga, Inu Yehova,

ganizirani za kusisima kwanga

2Mverani kulira kwanga kofuna thandizo,

Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,

pakuti kwa Inu, ine ndikupemphera.

3Mmawa, Yehova mumamva mawu anga;

Mmawa ndimayala zopempha zanga pamaso panu

ndi kudikira mwachiyembekezo.

4Inu si Mulungu amene mumasangalala ndi zoyipa;

choyipa sichikhala pamaso panu.

5Onyada sangathe kuyima pamaso panu;

Inu mumadana ndi onse ochita zoyipa.

6Mumawononga iwo amene amanena mabodza;

anthu akupha ndi achinyengo,

Yehova amanyansidwa nawo.

7Koma Ine, mwa chifundo chanu chachikulu,

ndidzalowa mʼNyumba yanu;

mwa ulemu ndidzaweramira pansi

kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera.

8Tsogolereni Inu Yehova, mwa chilungamo chanu

chifukwa cha adani anga ndipo

wongolani njira yanu pamaso panga.

9Palibe mawu ochokera mʼkamwa mwawo amene angadalirike;

mtima wawo wadzaza ndi chiwonongeko.

Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;

ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.

10Lengezani kuti ndi olakwa, Inu Mulungu!

Zochita zawo zoyipa zikhale kugwa kwawo.

Achotseni pamaso panu chifukwa cha machimo awo ambiri,

pakuti awukira Inu.

11Koma lolani kuti onse amene apeza chitetezo mwa Inu akondwere;

lolani kuti aziyimba nthawi zonse chifukwa cha chimwemwe.

Aphimbeni ndi chitetezo chanu,

iwo amene amakonda dzina lanu akondwere mwa Inu.

12Ndithu, Inu Yehova, mumadalitsa olungama;

mumawazungulira ndi kukoma mtima kwanu ngati chishango.

Священное Писание

Забур 5:1-13

Песнь 5

1Дирижёру хора. Для свирелей. Песнь Давуда.

2Услышь слова мои, Вечный,

пойми стенания мои!

3Внемли крику о помощи,

мой Царь и мой Бог,

ведь я молюсь Тебе!

4Утром, Вечный, Ты услышишь мой голос,

утром предстану с мольбой перед Тобою

и замру в ожидании.

5Ты не Бог, желающий беззакония,

зло не сможет обитать с Тобой.

6Надменные не устоят перед Тобой,

всех делающих зло Ты ненавидишь.

7Ты погубишь говорящих ложь;

кровожадных и коварных гнушается Вечный.

8Но я по великой милости Твоей

войду в дом Твой,

поклонюсь в святом храме Твоём

в страхе перед Тобой.

9Веди меня, Вечный, в праведности Твоей,

так как у меня много врагов;

уровняй предо мной путь,

по которому мне идти.

10Ведь ни одному слову из уст их верить нельзя,

сердце их исполнено пагубы.

Гортань их – открытая могила,

языком своим они льстят.

11Осуди их, Всевышний!

Пусть падут из-за козней своих!

Из-за многих грехов их отвергни их,

ведь они восстали против Тебя.

12Но пусть возрадуются все надеющиеся на Тебя,

пусть вечно поют от радости!

Окажи им Своё покровительство,

чтобы возрадовались все любящие имя Твоё.

13Ведь Ты благословляешь праведника, Вечный,

как щитом, окружаешь его благосклонностью.