Masalimo 48 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 48:1-14

Salimo 48

Nyimbo. Salimo la ana a Kora.

1Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando

mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.

2Lokongola mu utali mwake,

chimwemwe cha dziko lonse lapansi.

Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni,

mzinda wa Mfumu yayikulu.

3Mulungu ali mu malinga ake;

Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.

4Pamene mafumu anasonkhana pamodzi,

pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,

5iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri;

anathawa ndi mantha aakulu.

6Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera,

ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.

7Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi

zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.

8Monga momwe tinamvera,

kotero ife tinaona

mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse,

mu mzinda wa Mulungu wathu.

Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.

9Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu,

ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.

10Monga dzina lanu, Inu Mulungu,

matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi

dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.

11Phiri la Ziyoni likukondwera,

midzi ya Yuda ndi yosangalala

chifukwa cha maweruzo anu.

12Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo,

werengani nsanja zake.

13Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake,

penyetsetsani malinga ake,

kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.

14Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha;

Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

La Bible du Semeur

Psaumes 48:1-15

La cité de Dieu

1Cantique. Un psaume des Qoréites48.1 Voir note 42.1..

2Oui, l’Eternel est grand ! ╵Il est bien digne de louanges

dans la cité de notre Dieu, ╵sur sa montagne sainte.

3Colline magnifique, ╵joie de la terre entière,

mont de Sion, ╵tu es le véritable nord : ╵la demeure de Dieu48.3 L’hébreu a : les extrémités du Tsaphôn, ce qui peut se comprendre de manière géographique : du côté du nord, ou religieuse : le Tsaphôn était une montagne sacrée où, selon la religion phénicienne, Baal résidait.,

la cité du grand roi !

4Dieu, dans les palais de Sion,

se fait connaître ╵comme une forteresse.

5Car voici que les rois ╵s’étaient tous réunis ;

et ensemble, ils marchaient contre elle.

6Quand ils l’ont vue, ╵pris de stupeur,

épouvantés, ╵ils se sont tous enfuis !

7Un tremblement ╵les a saisis sur place,

pareil à la douleur ╵de la femme en travail.

8On aurait dit le vent de l’est

quand il vient fracasser ╵les bateaux au long cours.

9Ce que nous avions entendu, ╵nous l’avons vu nous-mêmes

dans la cité de l’Eternel, ╵le Seigneur des armées célestes,

dans la cité de notre Dieu.

Et pour toujours, ╵Dieu l’établit solidement.

Pause

10Nous méditons, ô Dieu, ╵sur ton amour,

au milieu de ton temple.

11Comme ta renommée,

ta louange a atteint ╵les confins de la terre.

Car par ta main tu accomplis ╵de nombreux actes de justice.

12Que le mont de Sion jubile.

Que, dans les villes de Juda, ╵on soit dans l’allégresse,

à cause de tes jugements !

13Tournez tout autour de Sion ╵et longez son enceinte,

comptez ses tours !

14Admirez ses remparts,

et passez en revue ╵chacun de ses palais

pour pouvoir annoncer ╵à la génération suivante

15que ce Dieu-là est notre Dieu ╵à tout jamais, ╵et éternellement,

il sera notre guide ╵jusqu’à la mort.