Masalimo 45 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 45:1-17

Salimo 45

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.

1Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma

pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;

lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.

2Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse

ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,

popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.

3Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;

mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.

4Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso

mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;

dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.

5Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,

mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.

6Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;

ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.

7Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu

pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.

8Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;

kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu

nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.

9Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;

ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.

10Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;

iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.

11Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;

mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.

12Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,

amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.

13Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,

chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.

14Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;

anamwali okhala naye akumutsatira

ndipo abweretsedwa kwa inu.

15Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;

akulowa mʼnyumba yaufumu.

16Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;

udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.

17Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;

choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

New International Reader’s Version

Psalm 45:1-17

Psalm 45

For the director of music. A maskil of the Sons of Korah. A wedding song to the tune of “Lilies.”

1My heart is full of beautiful words

as I say my poem for the king.

My tongue is like the pen of a skillful writer.

2You are the most excellent of men.

Your lips have been given the ability to speak gracious words.

God has blessed you forever.

3Mighty one, put your sword at your side.

Put on glory and majesty as if they were your clothes.

4In your majesty ride out with power

to fight for what is true, humble and fair.

Let your right hand do wonderful things.

5Shoot your sharp arrows into the hearts of your enemies.

Let the nations come under your control.

6Your throne is the very throne of God.

Your kingdom will last for ever and ever.

You will rule by treating everyone fairly.

7You love what is right and hate what is evil.

So your God has placed you above your companions.

He has filled you with joy by pouring the sacred oil on your head.

8Myrrh and aloes and cassia make all your robes smell good.

In palaces decorated with ivory

the music played on stringed instruments makes you glad.

9Daughters of kings are among the women you honor.

At your right hand is the royal bride dressed in gold from Ophir.

10Royal bride, listen and pay careful attention.

Forget about your people and the home you came from.

11Let the king be charmed by your beauty.

Honor him. He is now your master.

12The people of Tyre will come with gifts.

Wealthy people will try to gain your favor.

13In her room, the princess looks glorious.

Her gown has gold threads running through it.

14Dressed in beautiful clothes, she is led to the king.

Her virgin companions follow her.

They have been brought to be with her.

15They are led in with joy and gladness.

They enter the palace of the king.

16Your sons will rule just as your father and grandfather did.

You will make them princes through the whole land.

17I will make sure that people will always remember you.

The nations will praise you for ever and ever.