Masalimo 38 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 38:1-22

Salimo 38

Salimo la Davide. Kupempha.

1Yehova musandidzudzule mutapsa mtima

kapena kundilanga muli ndi ukali.

2Pakuti mivi yanu yandilasa,

ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.

3Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa;

mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.

4Kulakwa kwanga kwandipsinja

ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.

5Mabala anga akuwola ndipo akununkha

chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.

6Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri;

tsiku lonse ndimangolira.

7Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika,

mulibe thanzi mʼthupi langa.

8Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu;

ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.

9Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye,

kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.

10Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha;

ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.

11Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga;

anansi anga akhala kutali nane.

12Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo,

oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga;

tsiku lonse amakonza zachinyengo.

13Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve,

monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;

14Ndakhala ngati munthu amene samva,

amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.

15Ndikudikira Inu Yehova;

mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.

16Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere

kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”

17Pakuti ndili pafupi kugwa,

ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.

18Ndikuvomereza mphulupulu zanga;

ndipo ndavutika ndi tchimo langa.

19Ambiri ndi adani anga amphamvu;

amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.

20Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino

amandinyoza pamene nditsatira zabwino.

21Inu Yehova, musanditaye;

musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.

22Bwerani msanga kudzandithandiza,

Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

Hoffnung für Alle

Psalm 38:1-23

Zermürbt von Krankheit und Schuld

1Ein Lied von David, um sich bei Gott in Erinnerung zu bringen.

2Herr, du lässt mich deinen Zorn spüren.

Ich flehe dich an: Strafe mich nicht länger!

3Deine Pfeile haben sich in mich hineingebohrt,

deine Hand drückt mich nieder.

4Weil ich unter deinem Strafgericht leide,

habe ich keine heile Stelle mehr am Körper.

Weil mich die Sünde anklagt, sind alle meine Glieder krank.

5Meine Schuld ist mir über den Kopf gewachsen.

Wie schwer ist diese Last! Ich breche unter ihr zusammen.

6Wie dumm war ich, dich zu vergessen!

Das habe ich nun davon: Meine Wunden eitern und stinken!

7Gekrümmt und von Leid zermürbt

schleppe ich mich in tiefer Trauer durch den Tag.

8Von Fieber bin ich geschüttelt,

die Haut ist mit Geschwüren übersät.

9Zerschlagen liege ich da, am Ende meiner Kraft.

Vor Verzweiflung kann ich nur noch stöhnen.

10Herr, du kennst meine Sehnsucht,

du hörst mein Seufzen!

11Mein Herz rast, ich bin völlig erschöpft,

und meine Augen versagen mir den Dienst.

12Meine Freunde und Nachbarn ziehen sich zurück

wegen des Unglücks, das über mich hereingebrochen ist.

Sogar meine Verwandten gehen mir aus dem Weg.

13Meine Todfeinde stellen mir Fallen,

sie wollen mich verleumden und zugrunde richten.

Ja, sie bringen mich in Verruf, wann immer sie nur können.

14Und ich? Ich tue so, als hätte ich nichts gehört;

ich schweige zu ihren Anklagen wie ein Stummer.

15Ich stelle mich taub

und gebe ihnen keine Antwort.

16Denn auf dich, Herr, hoffe ich,

du wirst ihnen die passende Antwort geben,

mein Herr und mein Gott!

17Lass nicht zu, dass sie über mich triumphieren

und sich über mein Unglück freuen!

18Es fehlt nicht mehr viel, und ich liege am Boden,

ständig werde ich von Schmerzen gequält.

19Ich bekenne dir meine Schuld,

denn meine Sünde macht mir schwer zu schaffen.

20Übermächtig sind meine Feinde, und es gibt viele,

die mich ohne jeden Grund hassen.

21Sie vergelten mir Gutes mit Bösem und feinden mich an,

weil ich das Gute tun will.

22Herr, verlass mich nicht!

Mein Gott, bleib nicht fern von mir!

23Komm und hilf mir schnell!

Du bist doch mein Herr und mein Retter!