Masalimo 34 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 34:1-22

Salimo 34

Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka.

1Ndidzayamika Yehova nthawi zonse;

matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.

2Moyo wanga udzanyadira Yehova;

anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.

3Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine;

tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.

4Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha;

anandilanditsa ku mantha anga onse.

5Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira;

nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.

6Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva;

Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.

7Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye

ndi kuwalanditsa.

8Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino;

wodala munthu amene amathawira kwa Iye.

9Wopani Yehova inu oyera mtima ake,

pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.

10Mikango itha kulefuka ndi kumva njala

koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.

11Bwerani ana anga, mundimvere;

ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.

12Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake

ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,

13asunge lilime lake ku zoyipa

ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.

14Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;

funafuna mtendere ndi kuwulondola.

15Maso a Yehova ali pa olungama

ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;

16nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa,

kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.

17Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva;

Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.

18Yehova ali pafupi kwa osweka mtima

ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.

19Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri,

Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,

20Iye amateteza mafupa ake onse,

palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.

21Choyipa chidzapha anthu oyipa;

adani a olungama adzapezeka olakwa.

22Yehova amawombola atumiki ake;

aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.

Nova Versão Internacional

Salmos 34:1-22

Salmo 3434 O salmo 34 é um poema organizado em ordem alfabética, no hebraico.

De Davi, quando ele se fingiu de louco diante de Abimeleque—que o expulsou—e depois partiu.

1Bendirei o Senhor o tempo todo!

Os meus lábios sempre o louvarão.

2Minha alma se gloriará no Senhor;

ouçam os oprimidos e se alegrem.

3Proclamem a grandeza do Senhor comigo;

juntos exaltemos o seu nome.

4Busquei o Senhor, e ele me respondeu;

livrou-me de todos os meus temores.

5Os que olham para ele estão radiantes de alegria;

seu rosto jamais mostrará decepção.

6Este pobre homem clamou,

e o Senhor o ouviu;

e o libertou de todas as suas tribulações.

7O anjo do Senhor é sentinela ao redor

daqueles que o temem, e os livra.

8Provem e vejam como o Senhor é bom.

Como é feliz o homem que nele se refugia!

9Temam o Senhor, vocês que são os seus santos,

pois nada falta aos que o temem.

10Os leões34.10 A Septuaginta e a Versão Siríaca dizem ricos. podem passar necessidade e fome,

mas os que buscam o Senhor de nada têm falta.

11Venham, meus filhos, ouçam-me;

eu ensinarei a vocês o temor do Senhor.

12Quem de vocês quer amar a vida

e deseja ver dias felizes?

13Guarde a sua língua do mal

e os seus lábios da falsidade.

14Afaste-se do mal e faça o bem;

busque a paz com perseverança.

15Os olhos do Senhor voltam-se para os justos

e os seus ouvidos estão atentos ao seu grito de socorro;

16o rosto do Senhor volta-se contra os que praticam o mal,

para apagar da terra a memória deles.

17Os justos clamam, o Senhor os ouve

e os livra de todas as suas tribulações.

18O Senhor está perto dos que têm o coração quebrantado

e salva os de espírito abatido.

19O justo passa por muitas adversidades,

mas o Senhor o livra de todas;

20protege todos os seus ossos;

nenhum deles será quebrado.

21A desgraça matará os ímpios;34.21 Ou Os ímpios serão mortos nas suas próprias maldades;

os que odeiam o justo serão condenados.

22O Senhor redime a vida dos seus servos;

ninguém que nele se refugia será condenado.