Salimo 34
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka.
1Ndidzayamika Yehova nthawi zonse;
matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2Moyo wanga udzanyadira Yehova;
anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine;
tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha;
anandilanditsa ku mantha anga onse.
5Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira;
nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva;
Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye
ndi kuwalanditsa.
8Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino;
wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9Wopani Yehova inu oyera mtima ake,
pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10Mikango itha kulefuka ndi kumva njala
koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11Bwerani ana anga, mundimvere;
ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake
ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13asunge lilime lake ku zoyipa
ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;
funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15Maso a Yehova ali pa olungama
ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa,
kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva;
Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18Yehova ali pafupi kwa osweka mtima
ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri,
Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20Iye amateteza mafupa ake onse,
palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21Choyipa chidzapha anthu oyipa;
adani a olungama adzapezeka olakwa.
22Yehova amawombola atumiki ake;
aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.
Псалам 34
Давидов. Када се Давид претварао да је луд пред Авимелехом. Овај га је, затим, отерао, па је Давид отишао.
1Благосиљаћу Господа непрестано,
стално ће га усне моје хвалити.
2Хвалиће се Господом моја душа;
нека чују понизни, нека се радују.
3Величајте са мном Господа,
заједно му узвисујмо име.
4Тражио сам Господа, и он ми одговори,
од свих ме је страхова избавио.
5Ведри су они који гледају у њега,
лице се њихово неће постидети.
6Кад је овај сиромах вапио, Господ га је чуо,
и од свих га је невоља избавио.
7Анђео Господњи табором окружује
оне који га се боје; избавља их.
8Искусите и видите да је Господ добар,
благо човеку што у њему уточиште нађе.
9Бојте се Господа, ви свети његови,
јер нема оскудице за оне који га се боје.
10И млади лавови трпе и гладују,
али онима што траже Господа,
њима добра никаквог не мањка.
11Дођите, о, децо, и чујте ме,
богобојазности ћу вас поучити.
12Који човек воли живот?
Ко жели да добре дане види?
13Нек се твој језик од зла уздржи,
нек ти усне не говоре лажи,
14зла се клони, а добро чини,
тражи мир и за њим ти иди.
15Очи Господње мотре на праведне,
и уши његове вапај им чују.
16Лице се Господње мршти на зликовце,
да са земље помен им истреби.
17Господ чује кад праведни завапе,
од свих невоља он их избавља.
18Близу је Господ онима са сломљеним срцем,
он спасава оне са клонулим духом.
19Многа зла сналазе праведника,
али Господ га избавља од свих.
20Он чува све кости његове,
ниједна му се неће поломити.
21Зло ће убити опакога,
а који мрзе праведника биће окривљени.
22Господ откупљује живот својих слугу;
неће бити крив нико ко у њему уточиште нађе.