Masalimo 31 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 31:1-24

Salimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;

musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;

mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.

2Tcherani khutu lanu kwa ine,

bwerani msanga kudzandilanditsa;

mukhale thanthwe langa lothawirapo,

linga lolimba kundipulumutsa ine.

3Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.

4Ndimasuleni mu msampha umene anditchera

pakuti ndinu pothawirapo panga.

5Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;

womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

6Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;

ine ndimadalira Yehova.

7Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu

popeza Inu munaona masautso anga

ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.

8Inu simunandipereke kwa mdani

koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

9Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;

maso anga akulefuka ndi chisoni,

mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.

10Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima

ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;

mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,

ndipo mafupa anga akulefuka.

11Chifukwa cha adani anga onse,

ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;

ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.

Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.

12Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;

ndakhala ngati mʼphika wosweka.

13Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;

zoopsa zandizungulira mbali zonse;

iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,

kuti atenge moyo wanga.

14Koma ndikudalira Inu Yehova;

ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

15Masiku anga ali mʼmanja mwanu;

ndipulumutseni kwa adani anga

ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.

16Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;

pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.

17Yehova musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndalirira kwa Inu;

koma oyipa achititsidwe manyazi

ndipo agone chete mʼmanda.

18Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,

pakuti chifukwa cha kunyada

ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

20Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,

kuwateteza ku ziwembu za anthu;

mʼmalo anu okhalamo mumawateteza

kwa anthu owatsutsa.

21Matamando akhale kwa Yehova,

pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine

pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.

22Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,

“Ine ndachotsedwa pamaso panu!”

Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga

pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23Kondani Yehova oyera mtima ake onse!

Yehova amasunga wokhulupirika

koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.

24Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,

inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

Nova Versão Internacional

Salmos 31:1-24

Salmo 31

Para o mestre de música. Salmo davídico.

1Em ti, Senhor, me refugio;

nunca permitas que eu seja humilhado;

livra-me pela tua justiça.

2Inclina os teus ouvidos para mim,

vem livrar-me depressa!

Sê minha rocha de refúgio,

uma fortaleza poderosa para me salvar.

3Sim, tu és a minha rocha e a minha fortaleza;

por amor do teu nome, conduze-me e guia-me.

4Tira-me da armadilha que me prepararam,

pois tu és o meu refúgio.

5Nas tuas mãos entrego o meu espírito;

resgata-me, Senhor, Deus da verdade.

6Odeio aqueles que se apegam a ídolos inúteis;

eu, porém, confio no Senhor.

7Exultarei com grande alegria por teu amor,

pois viste a minha aflição

e conheceste a angústia da minha alma.

8Não me entregaste nas mãos dos meus inimigos;

deste-me segurança e liberdade.31.8 Hebraico: puseste os meus pés num lugar espaçoso.

9Misericórdia, Senhor! Estou em desespero!

A tristeza me consome

a vista, o vigor e o apetite31.9 Ou os olhos, a garganta e o ventre.

10Minha vida é consumida pela angústia,

e os meus anos pelo gemido;

minha aflição31.10 Ou culpa esgota as minhas forças,

e os meus ossos se enfraquecem.

11Por causa de todos os meus adversários,

sou motivo de ultraje para os meus vizinhos

e de medo para os meus amigos;

os que me veem na rua fogem de mim.

12Sou esquecido por eles como se estivesse morto;

tornei-me como um pote quebrado.

13Ouço muitos cochicharem a meu respeito;

o pavor me domina,

pois conspiram contra mim,

tramando tirar-me a vida.

14Mas eu confio em ti, Senhor,

e digo: Tu és o meu Deus.

15O meu futuro está nas tuas mãos;

livra-me dos meus inimigos

e daqueles que me perseguem.

16Faze o teu rosto resplandecer sobre31.16 Isto é, mostra a tua bondade para com. o teu servo;

salva-me por teu amor leal.

17Não permitas que eu seja humilhado, Senhor,

pois tenho clamado a ti;

mas que os ímpios sejam humilhados,

e calados fiquem no Sheol31.17 Essa palavra pode ser traduzida por sepultura, profundezas, ou morte..

18Sejam emudecidos os seus lábios mentirosos,

pois com arrogância e desprezo

humilham os justos.

19Como é grande a tua bondade,

que reservaste para aqueles que te temem,

e que, à vista dos homens,

concedes àqueles que se refugiam em ti!

20No abrigo da tua presença os escondes

das intrigas dos homens;

na tua habitação os proteges

das línguas acusadoras.

21Bendito seja o Senhor,

pois mostrou o seu maravilhoso amor para comigo

quando eu estava numa cidade cercada.

22Alarmado, eu disse:

Fui excluído da tua presença!

Contudo, ouviste as minhas súplicas

quando clamei a ti por socorro.

23Amem o Senhor, todos vocês, os seus santos!

O Senhor preserva os fiéis,

mas aos arrogantes dá o que merecem.

24Sejam fortes e corajosos,

todos vocês que esperam no Senhor!