Masalimo 31 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 31:1-24

Salimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;

musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;

mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.

2Tcherani khutu lanu kwa ine,

bwerani msanga kudzandilanditsa;

mukhale thanthwe langa lothawirapo,

linga lolimba kundipulumutsa ine.

3Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.

4Ndimasuleni mu msampha umene anditchera

pakuti ndinu pothawirapo panga.

5Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;

womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

6Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;

ine ndimadalira Yehova.

7Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu

popeza Inu munaona masautso anga

ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.

8Inu simunandipereke kwa mdani

koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

9Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;

maso anga akulefuka ndi chisoni,

mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.

10Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima

ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;

mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,

ndipo mafupa anga akulefuka.

11Chifukwa cha adani anga onse,

ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;

ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.

Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.

12Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;

ndakhala ngati mʼphika wosweka.

13Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;

zoopsa zandizungulira mbali zonse;

iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,

kuti atenge moyo wanga.

14Koma ndikudalira Inu Yehova;

ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

15Masiku anga ali mʼmanja mwanu;

ndipulumutseni kwa adani anga

ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.

16Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;

pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.

17Yehova musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndalirira kwa Inu;

koma oyipa achititsidwe manyazi

ndipo agone chete mʼmanda.

18Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,

pakuti chifukwa cha kunyada

ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

20Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,

kuwateteza ku ziwembu za anthu;

mʼmalo anu okhalamo mumawateteza

kwa anthu owatsutsa.

21Matamando akhale kwa Yehova,

pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine

pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.

22Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,

“Ine ndachotsedwa pamaso panu!”

Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga

pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23Kondani Yehova oyera mtima ake onse!

Yehova amasunga wokhulupirika

koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.

24Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,

inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

New International Version – UK

Psalms 31:1-24

Psalm 31In Hebrew texts 31:1-24 is numbered 31:2-25.

For the director of music. A psalm of David.

1In you, Lord, I have taken refuge;

let me never be put to shame;

deliver me in your righteousness.

2Turn your ear to me,

come quickly to my rescue;

be my rock of refuge,

a strong fortress to save me.

3Since you are my rock and my fortress,

for the sake of your name lead and guide me.

4Keep me free from the trap that is set for me,

for you are my refuge.

5Into your hands I commit my spirit;

deliver me, Lord, my faithful God.

6I hate those who cling to worthless idols;

as for me, I trust in the Lord.

7I will be glad and rejoice in your love,

for you saw my affliction

and knew the anguish of my soul.

8You have not given me into the hands of the enemy

but have set my feet in a spacious place.

9Be merciful to me, Lord, for I am in distress;

my eyes grow weak with sorrow,

my soul and body with grief.

10My life is consumed by anguish

and my years by groaning;

my strength fails because of my affliction,31:10 Or guilt

and my bones grow weak.

11Because of all my enemies,

I am the utter contempt of my neighbours

and an object of dread to my closest friends –

those who see me on the street flee from me.

12I am forgotten as though I were dead;

I have become like broken pottery.

13For I hear many whispering,

‘Terror on every side!’

They conspire against me

and plot to take my life.

14But I trust in you, Lord;

I say, ‘You are my God.’

15My times are in your hands;

deliver me from the hands of my enemies,

from those who pursue me.

16Let your face shine on your servant;

save me in your unfailing love.

17Let me not be put to shame, Lord,

for I have cried out to you;

but let the wicked be put to shame

and be silent in the realm of the dead.

18Let their lying lips be silenced,

for with pride and contempt

they speak arrogantly against the righteous.

19How abundant are the good things

that you have stored up for those who fear you,

that you bestow in the sight of all,

on those who take refuge in you.

20In the shelter of your presence you hide them

from all human intrigues;

you keep them safe in your dwelling

from accusing tongues.

21Praise be to the Lord,

for he showed me the wonders of his love

when I was in a city under siege.

22In my alarm I said,

‘I am cut off from your sight!’

Yet you heard my cry for mercy

when I called to you for help.

23Love the Lord, all his faithful people!

The Lord preserves those who are true to him,

but the proud he pays back in full.

24Be strong and take heart,

all you who hope in the Lord.