Masalimo 28 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 28:1-9

Salimo 28

Salimo la Davide.

1Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;

musakhale osamva kwa ine.

Pakuti mukapitirira kukhala chete,

ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

2Imvani kupempha chifundo kwanga

pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,

pomwe ndikukweza manja anga

kuloza ku malo anu oyeretsetsa.

3Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,

pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,

amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo

koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.

4Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo

ndi ntchito zawo zoyipa;

abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita

ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.

5Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,

ndi zimene manja ake anazichita,

Iye adzawakhadzula

ndipo sadzawathandizanso.

6Matamando apite kwa Yehova,

popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.

7Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;

mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe

ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

8Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,

linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.

9Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;

mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 28:1-9

Zabbuli 28

Zabbuli ya Dawudi.

128:1 a Zab 83:1 b Zab 88:4Nkukoowoola ggwe, Ayi Mukama, Olwazi lwange,

tolema kumpuliriza;

kubanga bw’onoonsiriikirira

nzija kuba nga bali abakkirira mu kinnya.

228:2 a Zab 138:2; 140:6 b Zab 5:7Owulire eddoboozi ery’okwegayirira kwange,

nga mpanise emikono gyange

okwolekera ekifo kyo ekisinga byonna obutukuvu,

nga nkukaabirira okunnyamba.

328:3 Zab 12:2; 26:9; Yer 9:8Tontwalira mu boonoonyi,

abakola ebibi;

abanyumya obulungi ne bannaabwe,

so ng’emitima gyabwe gijjudde bukyayi bwerere.

428:4 a 2Ti 4:14; Kub 22:12 b Kub 18:6Basasule ng’ebikolwa byabwe bwe biri,

n’olw’ebyambyone bye bakoze.

Basasule olwa byonna emikono gyabwe gye bisobezza,

obabonereze nga bwe basaanidde.

528:5 Is 5:12Olwokubanga tebafaayo ku mirimu gya Mukama,

oba ku ebyo bye yakola n’emikono gye,

alibazikiririza ddala,

era talibaddiramu.

6Atenderezebwe Mukama,

kubanga awulidde eddoboozi ly’okwegayirira kwange.

728:7 a Zab 18:1 b Zab 13:5 c Zab 40:3; 69:30Mukama ge maanyi gange,

era ye ngabo yange, ye gwe neesiga.

Bwe ntyo ne nyambibwa.

Omutima gwange gunaajaguzanga, ne mmuyimbira ennyimba ez’okumwebazanga.

828:8 Zab 20:6Mukama y’awa abantu be amaanyi,

era kye kiddukiro eky’obulokozi bw’oyo gwe yafukako amafuta.

928:9 a Ma 9:29; Ezr 1:4 b Is 40:11 c Ma 1:31; 32:11Olokole abantu bo, obawe omukisa abalonde bo.

Obakulemberenga ng’omusumba, era obawanirirenga emirembe gyonna.