Masalimo 28 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 28:1-9

Salimo 28

Salimo la Davide.

1Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;

musakhale osamva kwa ine.

Pakuti mukapitirira kukhala chete,

ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

2Imvani kupempha chifundo kwanga

pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,

pomwe ndikukweza manja anga

kuloza ku malo anu oyeretsetsa.

3Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,

pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,

amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo

koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.

4Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo

ndi ntchito zawo zoyipa;

abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita

ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.

5Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,

ndi zimene manja ake anazichita,

Iye adzawakhadzula

ndipo sadzawathandizanso.

6Matamando apite kwa Yehova,

popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.

7Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;

mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe

ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

8Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,

linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.

9Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;

mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

La Bible du Semeur

Psaumes 28:1-9

L’Eternel répond

1De David.

A toi, ô Eternel, ╵je fais appel ;

toi, mon rocher, ╵ne sois pas sourd ╵à ma requête.

Si tu restes muet,

je deviendrai pareil ╵à ceux qui s’en vont vers la tombe.

2Entends ma voix qui te supplie ╵quand je t’appelle à l’aide

en élevant mes mains28.2 Geste habituel de la prière en Israël (63.5 ; 134.2 ; 141.2 ; 1 R 8.22 ; Esd 9.5 ; Né 8.6 ; Es 1.15 ; 1 Tm 2.8). ╵en direction du lieu très saint ╵de ta demeure !

3Ne me fais pas subir ╵avec les criminels, ╵avec les malfaisants, ╵le sort qui leur est réservé ;

ces gens parlent de paix ╵à leur prochain, ╵avec le mal au fond du cœur.

4Oui, traite-les selon leurs actes ╵et leurs méfaits ;

oui, traite-les selon leurs œuvres,

fais retomber sur eux ╵ce qu’ils ont fait !

5Car ils ne tiennent aucun compte ╵des actes accomplis par l’Eternel

et de ses œuvres.

Que l’Eternel ╵fasse venir leur ruine ╵et qu’il ne les relève pas !

6Béni soit l’Eternel,

car il m’entend ╵lorsque je le supplie.

7L’Eternel est ma force, ╵mon bouclier.

En lui je me confie ; ╵il vient à mon secours.

Aussi mon cœur bondit de joie.

Je veux chanter pour le louer.

8L’Eternel est la force ╵de tous les siens28.8 En hébreu : d’eux. Une légère modification de l’hébreu permet de lire : de son peuple.,

il est la forteresse ╵où le roi qui a reçu l’onction de sa part ╵trouve la délivrance.

9O Eternel, ╵sauve ton peuple, ╵et bénis-le : ╵il est ton patrimoine.

Sois son berger, ╵et prends soin de lui pour toujours.