Masalimo 27 – CCL & TCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 27:1-14

Salimo 27

Salimo la Davide.

1Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;

ndidzaopa yani?

Yehova ndi linga la moyo wanga;

ndidzachita mantha ndi yani?

2Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane

kudzadya mnofu wanga,

pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo,

iwo adzapunthwa ndi kugwa.

3Ngakhale gulu lankhondo lindizinge,

mtima wanga sudzaopa.

Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane,

ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.

4Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,

ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:

kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova

masiku onse a moyo wanga,

ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,

ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.

5Pakuti pa tsiku la msautso

Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;

adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake

ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.

6Kotero mutu wanga udzakwezedwa

kuposa adani anga amene andizungulira;

pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe;

ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.

7Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova

mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.

8Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!”

Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.

9Musandibisire nkhope yanu,

musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo;

mwakhala muli thandizo langa.

Musandikane kapena kunditaya,

Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.

10Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya

Yehova adzandisamala.

11Phunzitseni njira yanu Inu Yehova,

munditsogolere mʼnjira yowongoka

chifukwa cha ondizunza.

12Musandipereke ku zokhumba za adani anga,

pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane

ndipo zikundiopseza.

13Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi;

ndidzaona ubwino wa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

14Dikirani pa Yehova;

khalani anyonga ndipo limbani mtima

nimudikire Yehova.

Tagalog Contemporary Bible

Salmo 27:1-14

Salmo 2727 Salmo 27 Ang unang mga salita sa Hebreo: Ang Salmo ni David.

Panalangin ng Pagtitiwala

1Ang Panginoon ang aking ilaw at Tagapagligtas.

Sino ang aking katatakutan?

Siya ang nagtatanggol sa akin kaya wala akong dapat katakutan.

2Kapag sinasalakay ako ng masasamang tao o ng aking mga kaaway upang patayin,

sila ang nabubuwal at natatalo!

3Kahit mapaligiran ako ng maraming kawal,

hindi ako matatakot.

Kahit salakayin nila ako,

magtitiwala ako sa Dios.

4Isang bagay ang hinihiling ko sa Panginoon, ito ang tanging ninanais ko:

na akoʼy manirahan sa kanyang templo habang akoʼy nabubuhay,

upang mamasdan ang kanyang kadakilaan,

at hilingin sa kanya ang kanyang patnubay.

5Sa oras ng kagipitan ay itatago niya ako sa kanyang templo,

at ilalagay niya ako sa ligtas na lugar.

6Kaya mananaig ako sa mga kaaway ko na nakapaligid sa akin.

Maghahandog ako sa templo ng Panginoon habang sumisigaw sa kagalakan,

umaawit at nagpupuri.

7Dinggin nʼyo Panginoon ang aking pagtawag.

Kahabagan nʼyo ako at sagutin ang aking dalangin.

8Panginoon, hinipo nʼyo ang aking puso na lumapit sa inyo,

kaya narito ako, lumalapit sa inyo.

9Huwag nʼyo po akong pagtaguan!

Ako na alipin nʼyo ay huwag nʼyong itakwil dahil sa inyong galit.

Kayo na laging tumutulong sa akin,

huwag nʼyo akong iwanan at pabayaan,

O Dios na aking Tagapagligtas.

10Iwanan man ako ng aking mga magulang,

kayo naman, Panginoon, ang mag-aalaga sa akin.

11Ituro nʼyo sa akin ang daang gusto nʼyong lakaran ko.

Patnubayan nʼyo ako sa tamang daan,

dahil sa mga kaaway ko na gusto akong gawan ng masama.

12Huwag nʼyo akong ibigay sa aking mga kaaway,

dahil akoʼy kanilang pinagbibintangan ng kasinungalingan,

at nais nilang akoʼy saktan.

13Ngunit naniniwala ako na mararanasan ko ang kabutihan nʼyo, Panginoon,

habang akoʼy nabubuhay dito sa mundo.

14Magtiwala kayo sa Panginoon!

Magpakatatag kayo at huwag mawalan ng pag-asa.

Magtiwala lamang kayo sa Panginoon!