Masalimo 26 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 26:1-12

Salimo 26

Salimo la Davide.

1Weruzeni Inu Yehova

pakuti ndakhala moyo wosalakwa.

Ndadalira Yehova

popanda kugwedezeka.

2Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,

santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;

3pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,

ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.

4Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,

kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.

5Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa

ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.

6Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga

ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,

7kulengeza mofuwula za matamando anu

ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.

8Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,

malo amene ulemerero wanu umapezekako.

9Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,

moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,

10amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,

dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.

11Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;

mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.

12Ndayima pa malo wopanda zovuta

ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.

Hoffnung für Alle

Psalm 26:1-12

Prüfe mich, Gott!

1Von David.

Verschaffe mir Recht, Herr, denn ich bin unschuldig!

Dir vertraue ich, nichts soll mich davon abbringen.

2Vor dir, Herr, kann ich nichts verbergen,

prüfe meine geheimsten Gedanken und Gefühle!

3Deine Liebe habe ich ständig vor Augen,

und deine Treue bestimmt mein Leben.

4Ich lasse mich nicht mit denen ein, die ein falsches Spiel treiben.

Von Heuchlern halte ich mich fern.

5Wenn sich Verbrecher zusammentun, bin ich nicht dabei;

mit Gottlosen will ich nichts zu tun haben.

6Ich wasche meine Hände zum Zeichen meiner Unschuld,

so darf ich mich deinem Altar nähern und ihn feierlich umschreiten.

7Dabei stimme ich ein Loblied an

und erzähle von all deinen Wundern.

8Herr, dein Haus ist erfüllt von deiner Herrlichkeit;

an diesem Ort hängt mein Herz.

9Bring mich nicht um wie die Sünder;

behandle mich nicht wie blutgierige Mörder!

10Wie viele Verbrechen haben sie auf dem Gewissen,

wie viel Bestechungsgeld ist durch ihre Hände gegangen!

11Aber ich habe mir nichts zuschulden kommen lassen.

Hab Erbarmen mit mir und erlöse mich!

12Jetzt stehe ich wieder auf sicherem Grund.

Herr, vor deiner Gemeinde will ich dich dafür preisen!