Masalimo 23 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 23:1-6

Salimo 23

Salimo la Davide.

1Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.

2Amandigoneka pa msipu wobiriwira,

amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,

3amatsitsimutsa moyo wanga.

Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo

chifukwa cha dzina lake.

4Ngakhale ndiyende

mʼchigwa cha mdima wakuda bii,

sindidzaopa choyipa,

pakuti Inu muli ndi ine;

chibonga chanu ndi ndodo yanu

zimanditonthoza.

5Mumandikonzera chakudya

adani anga akuona.

Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta;

chikho changa chimasefukira.

6Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata

masiku onse a moyo wanga,

ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova

kwamuyaya.

O Livro

Salmos 23:1-6

Salmo 23

Salmo de David.

1O Senhor é o meu Pastor,

por isso, nada me faltará.

2Faz-me descansar em verdes pastagens;

guia-me calmamente a ribeiros tranquilos.

3Dá novas forças à minha alma;

conduz-me pelos caminhos da justiça,

para que eu honre o seu bom nome.

4Se andar pelo escuro desfiladeiro da morte,

não terei medo, porque tu estás comigo;

a tua vara e o teu cajado me amparam.

5Preparas-me uma mesa maravilhosa,

mesmo na presença dos meus inimigos.

Unges a minha cabeça com óleo;

enches-me de abundantes bênçãos,

como uma taça que transborda.

6Sem dúvida que a tua bondade e a tua misericórdia

me hão de acompanhar todos os dias da minha vida.

Habitarei na tua casa para sempre.