Masalimo 22 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 22:1-31

Salimo 22

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide.

1Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?

Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?

Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?

2Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,

usikunso, ndipo sindikhala chete.

3Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;

ndinu matamando a Israeli.

4Pa inu makolo athu anadalira;

iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.

5Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.

Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.

6Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,

wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.

7Onse amene amandiona amandiseka;

amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti

8“Iyeyu amadalira Yehova,

musiyeni Yehovayo amulanditse.

Musiyeni Yehova amupulumutse

popeza amakondwera mwa Yehovayo.”

9Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.

Munachititsa kuti ndizikudalirani

ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.

10Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;

kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.

11Musakhale kutali ndi ine,

pakuti mavuto ali pafupi

ndipo palibe wina wondipulumutsa.

12Ngʼombe zazimuna zandizungulira;

ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.

13Mikango yobangula pokadzula nyama,

yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.

14Ine ndatayika pansi ngati madzi

ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.

Mtima wanga wasanduka phula;

wasungunuka mʼkati mwanga.

15Mphamvu zanga zauma ngati phale,

ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;

mwandigoneka mʼfumbi la imfa.

16Agalu andizungulira;

gulu la anthu oyipa landizinga.

Alasa manja ndi mapazi anga.

17Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse;

anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.

18Iwo agawana zovala zanga pakati pawo

ndi kuchita maere pa zovala zangazo.

19Koma Inu Yehova, musakhale kutali;

Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.

20Pulumutsani moyo wanga ku lupanga,

moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.

21Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango;

pulumutseni ku nyanga za njati.

22Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga;

ndidzakutamandani mu msonkhano.

23Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni!

Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni!

Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!

24Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza

kuvutika kwa wosautsidwayo;

Iye sanabise nkhope yake kwa iye.

Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.

25Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira.

Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.

26Osauka adzadya ndipo adzakhuta;

iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda.

Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!

27Malekezero onse a dziko lapansi

adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye,

ndipo mabanja a mitundu ya anthu

adzawerama pamaso pake,

28pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova

ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.

29Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira;

onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake;

iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.

30Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye;

mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.

31Iwo adzalengeza za chilungamo chake

kwa anthu amene pano sanabadwe

pakuti Iye wachita zimenezi.

New Serbian Translation

Псалми 22:1-31

Псалам 22

Хоровођи, по напеву кошута у зори. Давидов псалам.

1Боже мој, Боже мој, зашто си ме оставио?!

Далеко си од мога спасења,

и од речи вапаја мојега.

2Боже мој, вапим дању, а ти не одговараш;

ноћу, али нема ми одмора.

3А ти си онај Свети,

престо ти је на хвалама Израиљевим.

4У тебе су се наши преци уздали,

уздали се и ти их избави.

5Теби су вапили и избављени били,

у тебе се уздали и нису се осрамотили.

6А ја сам црв, а не човек,

ругло људима, презир народа.

7Ко год ме види, тај ми се руга,

цере ми се и машу главама:

8„У Господа се уздао, нека га он избави,

кад у њему радост налази.“

9Јер ти си ме извукао из утробе мајчине,

на грудима мајке дао ми починак.

10Теби сам предан од мајчина крила,

од утробе мајчине ти си Бог мој.

11Не удаљуј се од мене,

јер невоља је близу,

а помоћника нема.

12Окружише ме многи бикови,

бикови ме васански опколише.

13На мене су чељуст раширили,

као лав што раздире и риче.

14Попут воде живот ми истиче,

све су ми се кости разглавиле,

срце ми је ко восак постало,

и топи се у мојим грудима.

15Снага ми се као цреп сасуши,

језик ми је уз непце прионуо;

у смртни си ме прах ставио.

16Јер пси су ме, ево, опколили,

окружила ме чета зликоваца,

руке су ми и ноге пробили.

17Све кости своје избројати могу,

а они ме гледају и зуре у мене.

18Моје хаљине деле међу собом,

коцку бацају за моју одећу.

19Не удаљуј се од мене, Господе,

снаго моја, пожури ми у помоћ,

20душу моју избави од мача,

и мој живот од канџи паса.

21Избави ме од лавље чељусти,

и од рогова биволових!

22А ја ћу причати о твом имену браћи својој,

хвалићу те усред збора.

23Хвалите Господа, ви што га се бојите,

славите га, све семе Јаковљево,

сав род Израиљев, нек од њега стрепи!

24Јер патњу угњетеног није презрео,

нити му је постала одвратна,

није своје лице сакрио од њега,

него му је вапај услишио.

25О теби ћу певати на великом збору,

испунићу завете своје пред онима који га се боје.

26Понизни ће јести и бити сити,

хвалиће Господа који га траже.

Нека срца ваша живе довека!

27Сетиће се и вратити Господу,

сви крајеви земаљски,

пашће ничице пред тобом

сва племена народа.

28Јер Господње је Царство,

он влада над народима.

29Њему ће се клањати сви богати

и сити на земљи,

пред њим ће клекнути сви који у прах силазе,

којима се живот угасио.

30Потомство њему ће служити,

причаће о Господу будућем нараштају,

31доћи ће и објавити праведност његову

народу који се још није родио,

да је он то учинио.