Masalimo 22 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 22:1-31

Salimo 22

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide.

1Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?

Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?

Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?

2Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,

usikunso, ndipo sindikhala chete.

3Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;

ndinu matamando a Israeli.

4Pa inu makolo athu anadalira;

iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.

5Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.

Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.

6Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,

wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.

7Onse amene amandiona amandiseka;

amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti

8“Iyeyu amadalira Yehova,

musiyeni Yehovayo amulanditse.

Musiyeni Yehova amupulumutse

popeza amakondwera mwa Yehovayo.”

9Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.

Munachititsa kuti ndizikudalirani

ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.

10Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;

kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.

11Musakhale kutali ndi ine,

pakuti mavuto ali pafupi

ndipo palibe wina wondipulumutsa.

12Ngʼombe zazimuna zandizungulira;

ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.

13Mikango yobangula pokadzula nyama,

yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.

14Ine ndatayika pansi ngati madzi

ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.

Mtima wanga wasanduka phula;

wasungunuka mʼkati mwanga.

15Mphamvu zanga zauma ngati phale,

ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;

mwandigoneka mʼfumbi la imfa.

16Agalu andizungulira;

gulu la anthu oyipa landizinga.

Alasa manja ndi mapazi anga.

17Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse;

anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.

18Iwo agawana zovala zanga pakati pawo

ndi kuchita maere pa zovala zangazo.

19Koma Inu Yehova, musakhale kutali;

Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.

20Pulumutsani moyo wanga ku lupanga,

moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.

21Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango;

pulumutseni ku nyanga za njati.

22Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga;

ndidzakutamandani mu msonkhano.

23Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni!

Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni!

Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!

24Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza

kuvutika kwa wosautsidwayo;

Iye sanabise nkhope yake kwa iye.

Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.

25Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira.

Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.

26Osauka adzadya ndipo adzakhuta;

iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda.

Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!

27Malekezero onse a dziko lapansi

adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye,

ndipo mabanja a mitundu ya anthu

adzawerama pamaso pake,

28pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova

ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.

29Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira;

onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake;

iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.

30Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye;

mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.

31Iwo adzalengeza za chilungamo chake

kwa anthu amene pano sanabadwe

pakuti Iye wachita zimenezi.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 22:1-31

第 22 篇

苦難中的呼求和感恩

大衛的詩,交給樂長,調用「朝鹿」。

1我的上帝,我的上帝,

你為何離棄我?

為何遲遲不來救我,

不聽我的哀號呢?

2我的上帝啊,

我日夜不停地呼求,

你卻沒有回應。

3然而,你是聖潔的,

你的寶座設立在以色列人的頌讚之上。

4我們的祖先信靠你,

他們信靠你,

你就拯救他們。

5他們向你呼求,

就得到拯救;

他們信靠你,

就不會失望。

6但我好像不是人,只是一條蟲,

受盡人的羞辱和藐視。

7看見我的人都譏笑我,

他們撇著嘴、搖著頭說:

8「他信靠耶和華,

讓耶和華救他吧!

既然耶和華喜悅他,

讓耶和華拯救他吧!」

9耶和華啊,

是你使我從母腹中安然出生,

讓我在母親懷裡便倚靠你。

10我一出生就被交托在你手中,

你從我出母胎就是我的上帝。

11求你不要遠離我,

因為危難當頭,無人幫我。

12我被許多仇敵圍困,

他們像巴珊的公牛那樣強壯。

13他們張口要吞噬我,

如同吼叫著撕食獵物的獅子。

14我的力量如水消逝,

我的骨頭都脫了節,

我的心如蠟熔化。

15我的力量枯竭如焦土,

我的舌頭髮乾緊貼上顎。

你把我放在死亡的塵土中。

16惡人包圍我,猶如一群惡犬,

他們刺傷我的手腳。

17我身上的骨頭歷歷可見,

人們都幸災樂禍地看著我。

18他們分我的外衣,

又為我的內衣抽籤。

19耶和華啊,求你不要遠離我。

你是我的力量,

求你快來幫助我。

20求你救我逃脫刀劍之災,

從這些惡犬的利爪下拯救我的生命。

21求你救我脫離獅子的口,

使我脫離野牛的角。

22我要向眾弟兄傳揚你的名,

在會眾當中讚美你。

23敬畏耶和華的人啊,

你們都要讚美祂,

雅各的後裔都要尊崇祂的名,

以色列的後裔都要敬畏祂。

24因為祂沒有藐視、厭惡苦難中的人,

也沒有掩面不顧他們,

而是垂聽他們的呼求。

25我要在大會中讚美你,

在敬畏你的人面前履行我的誓言。

26窮苦人必得飽足,

尋求耶和華的人必讚美祂,

他們的心要永遠歡欣跳躍。

27普世都要心繫耶和華,歸向祂,

各國人民都要敬拜祂。

28因為耶和華是主宰,

祂統治列國。

29世上的富貴人要敬拜祂,

必歸塵土的世人都要敬拜祂。

30世世代代的人都要事奉祂,

傳揚主所行的奇事。

31他們也要向未來的世代傳講祂的公義作為。