Masalimo 22 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 22:1-31

Salimo 22

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide.

1Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?

Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?

Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?

2Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,

usikunso, ndipo sindikhala chete.

3Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;

ndinu matamando a Israeli.

4Pa inu makolo athu anadalira;

iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.

5Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.

Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.

6Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,

wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.

7Onse amene amandiona amandiseka;

amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti

8“Iyeyu amadalira Yehova,

musiyeni Yehovayo amulanditse.

Musiyeni Yehova amupulumutse

popeza amakondwera mwa Yehovayo.”

9Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.

Munachititsa kuti ndizikudalirani

ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.

10Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;

kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.

11Musakhale kutali ndi ine,

pakuti mavuto ali pafupi

ndipo palibe wina wondipulumutsa.

12Ngʼombe zazimuna zandizungulira;

ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.

13Mikango yobangula pokadzula nyama,

yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.

14Ine ndatayika pansi ngati madzi

ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.

Mtima wanga wasanduka phula;

wasungunuka mʼkati mwanga.

15Mphamvu zanga zauma ngati phale,

ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;

mwandigoneka mʼfumbi la imfa.

16Agalu andizungulira;

gulu la anthu oyipa landizinga.

Alasa manja ndi mapazi anga.

17Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse;

anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.

18Iwo agawana zovala zanga pakati pawo

ndi kuchita maere pa zovala zangazo.

19Koma Inu Yehova, musakhale kutali;

Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.

20Pulumutsani moyo wanga ku lupanga,

moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.

21Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango;

pulumutseni ku nyanga za njati.

22Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga;

ndidzakutamandani mu msonkhano.

23Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni!

Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni!

Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!

24Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza

kuvutika kwa wosautsidwayo;

Iye sanabise nkhope yake kwa iye.

Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.

25Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira.

Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.

26Osauka adzadya ndipo adzakhuta;

iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda.

Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!

27Malekezero onse a dziko lapansi

adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye,

ndipo mabanja a mitundu ya anthu

adzawerama pamaso pake,

28pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova

ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.

29Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira;

onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake;

iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.

30Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye;

mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.

31Iwo adzalengeza za chilungamo chake

kwa anthu amene pano sanabadwe

pakuti Iye wachita zimenezi.

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom 22:1-31

Dwom 22

Dawid dwom.

1Me Onyankopɔn, me Onyankopɔn, adɛn enti na woagya me?

Adɛn enti na me nkwagyeɛ ne wo ntam aware,

adɛn na mʼapinisie nsɛm ne wo ntam aware?

2Ao me Onyankopɔn, mesu frɛ wo awia, nanso wonnye me so,

mefrɛ wo anadwo, nanso mennya ɔhome.

3Nanso, wɔasi wo ɔhene sɛ Ɔkronkronni;

wo na Israel kamfo woɔ.

4Wo mu na yɛn agyanom de wɔn werɛ hyɛeɛ;

wɔgyee wo diiɛ, na wogyee wɔn.

5Wɔsu frɛɛ wo na wogyee wɔn,

wɔde wɔn ho too wo so na woanni wɔn hwammɔ.

6Nanso meyɛ ɔsonsono, na menyɛ onipa

nnipa bɔ me ahohora na wɔbu me animtiaa.

7Obiara a ɔhunu me di me ho fɛw;

wɔtwa me adapaa, woso wɔn ti ka sɛ:

8“Ɔde ne ho to Awurade so;

ma Awurade mmɛgye no.

Ma ɔmmɛboa no,

ɛfiri sɛ ɔwɔ ne mu anigyeɛ.”

9Wo na woyii me firii awotwaa mu baeɛ

na womaa mede me ho too wo so

ɛberɛ a metua me maame nufoɔ ano mpo.

10Ɛfiri mʼawoɔ mu na wɔde me too wo soɔ;

ɛfiri me maame yafunu mu, woayɛ me Onyankopɔn.

11Ntwe wo ho mfiri me ho!

Ɛfiri sɛ amaneɛ abɛn

na ɔboafoɔ nni baabi.

12Anantwinini bebree atwa me ho ahyia;

Basan anantwinini a wɔn ho yɛ den atwa me ho ahyia.

13Gyata a wɔbobom na wɔtete wɔn ahaboa mu

abuebue wɔn anom tɛtrɛɛ de kyerɛ me.

14Wɔahwie me agu sɛ nsuo,

na me nnompe nyinaa ahodwo.

Mʼakoma adane ayɛ sɛ nku;

anane afiri me mu.

15Mʼahoɔden awe te sɛ kyɛmferɛ mu.

Na me tɛkrɛma atare mʼanom.

Wode me ato owuo mfuturo mu.

16Nkraman atwa me ho ahyia

nnebɔneyɛfoɔ kuo atwa me ho ahyia,

wɔahwire me nsa ne me nan mu.

17Mɛtumi akan me nnompe nyinaa;

Mʼatamfoɔ di me nhwɛhaa na wɔsere me.

18Wɔkyɛ me atadeɛ mu fa,

na wɔbɔ me ntoma so ntonto.

19Na wo, Ao Awurade, ntwe wo ho.

Ao mʼAhoɔden bra ntɛm bɛboa me.

20Gye me kra firi akofena ano;

gye me nkwa a ɛsom bo no firi nkraman tumi ase.

21Gye me nkwa firi gyata anom;

gye me firi ɛkoɔ mmɛn so.

22Mɛbɔ wo din akyerɛ me nuanom;

mɛkamfo wo wɔ wɔn a wɔahyia hɔ no nyinaa anim.

23Monkamfo Awurade, mo a mosuro no no!

Mo a moyɛ Yakob asefoɔ, monhyɛ no animuonyam!

Mo Israel asefoɔ nyinaa, monni no ni!

24Ɔmmuu nʼani nguu

ɔmanehunufoɔ ateetee so,

ɔmfaa nʼanim nhintaa no;

na mmom watie ne sufrɛ a ɔde repɛ mmoa.

25Me botaeɛ a mede yi wo ayɛ wɔ badwa mu no firi wo;

mɛdi me bɔhyɛ so wɔ wɔn a wɔsuro wo no anim.

26Ahiafoɔ bɛdidi na wɔamee;

wɔn a wɔhwehwɛ Awurade bɛyi no ayɛ.

Mo akoma nnya nkwa daa.

27Asase ano nyinaa

bɛkae akɔ Awurade nkyɛn,

na amanaman no mmusua nyinaa

bɛkoto nʼanim,

28ɛfiri sɛ ahennie wɔ Awurade

na ɔdi amanaman so ɔhene.

29Asase so adefoɔ nyinaa bɛdidi na wɔasɔre no;

wɔn a wɔkɔ dɔteɛ mu nyinaa bɛbu nkotodwe nʼanim,

wɔn a wɔrentumi mma nkwa mu.

30Nkyirimma nyinaa bɛsom no;

wɔbɛka Awurade ho asɛm akyerɛ awoɔ ntoatoasoɔ a ɛdidi soɔ.

31Wɔbɛka ne tenenee akyerɛ

nnipa a wɔnnya nwoo wɔn

ɛfiri sɛ ɔno na wayɛ.