Masalimo 21 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 21:1-13

Salimo 21

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu,

chimwemwe chake nʼchachikuludi pa kupambana kumene mumapereka!

2Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake

ndipo simunayimane zopempha za pa milomo yake.

Sela

3Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka

ndipo munayiveka chipewa chaufumu chagolide weniweni pa mutu wake.

4Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa

masiku ochuluka kwamuyaya.

5Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu;

Inu mwapereka pa iyo ulemerero ndi ufumu.

6Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya,

Inu mwayipatsa chisangalalo ndi chimwemwe chimene chili pamaso panu.

7Pakuti mfumu imadalira Yehova;

kudzera mʼchikondi chake chosatha cha Wammwambamwamba,

iyo sidzagwedezeka.

8Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse;

dzanja lanu lamanja lidzagwira adani anu.

9Pa nthawi ya kuonekera kwanu

mudzawasandutsa ngʼanjo yamoto yotentha.

Mu ukali wake Yehova adzawameza,

ndipo moto wake udzawatha.

10Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi,

zidzukulu zawo pakati pa anthu.

11Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo

sadzapambana;

12pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo

pamene mudzawaloza ndi mivi yanu.

13Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu,

ife tidzayimba nyimbo ndi kutamanda mphamvu yanu.

Het Boek

Psalmen 21:1-14

1Een psalm van David voor de koordirigent.

2Here, de koning verheugt zich

over uw macht,

met vreugde spreekt hij

over het heil dat U geeft.

3U vervulde

zijn grootste wens.

Wat hij U vroeg,

hebt U hem niet geweigerd.

4U komt hem tegemoet

met overvloed

en geeft hem

een prachtige gouden kroon.

5Hij vroeg U

te mogen leven,

dat stond U hem toe

tot in hoge ouderdom.

6Dankzij U

is hij beroemd en geëerd.

U gaf hem

aanzien en majesteit.

7U zegent hem rijk

en geeft hem

een hart vol blijdschap.

8Allemaal omdat de koning

op de Here vertrouwt,

door de goedheid en de liefde

van God, de Allerhoogste,

faalt hij niet.

9Here, U weet uw vijanden te vinden.

Wie U haten,

zullen niet aan U ontkomen.

10Wanneer U komt, Here,

zullen zij door uw toorn verbranden,

U zult hen vernietigen.

In het vuur zullen zij omkomen.

11Zelfs hun kinderen

zult U wegdoen van deze aarde

en hun nageslacht zal niet bestaan.

12Als zij proberen U kwaad te doen

en slechte plannen maken,

zal dat hun niet lukken.

13U laat hen vluchten,

U richt uw pijlen op hun gezicht.

14Toon uw kracht, Here,

dan zullen wij

liederen zingen tot uw eer.