Masalimo 2 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 2:1-12

Salimo 2

1Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu?

Akonzekeranji zopanda pake anthu?

2Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo;

ndipo olamulira asonkhana pamodzi

kulimbana ndi Ambuye

ndi wodzozedwa wakeyo.

3Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo

ndipo titaye zingwe zawo.”

4Wokhala mmwamba akuseka;

Ambuye akuwanyoza iwowo.

5Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake

ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,

6“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga

pa Ziyoni, phiri langa loyera.”

7Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula:

Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga;

lero Ine ndakhala Atate ako.

8Tandipempha,

ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako;

malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.

9Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo;

udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”

10Kotero, inu mafumu, chenjerani;

chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.

11Tumikirani Yehova mwa mantha

ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.

12Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye;

kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu,

pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa.

Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

Nova Versão Internacional

Salmos 2:1-12

Salmo 2

1Por que se amotinam2.1 A Septuaginta diz se enfurecem. as nações

e os povos tramam em vão?

2Os reis da terra tomam posição

e os governantes conspiram unidos

contra o Senhor e contra o seu ungido, e dizem:

3“Façamos em pedaços as suas correntes,

lancemos de nós as suas algemas!”

4Do seu trono nos céus

o Senhor põe-se a rir e caçoa deles.

5Em sua ira os repreende

e em seu furor os aterroriza, dizendo:

6“Eu mesmo estabeleci o meu rei

em Sião, no meu santo monte”.

7Proclamarei o decreto do Senhor:

Ele me disse: “Tu és meu filho;

eu hoje te gerei.

8Pede-me, e te darei as nações como herança

e os confins da terra como tua propriedade.

9Tu as quebrarás com vara de ferro2.9 Ou as governarás com cetro de ferro

e as despedaçarás como a um vaso de barro”.

10Por isso, ó reis, sejam prudentes;

aceitem a advertência, autoridades da terra.

11Adorem o Senhor com temor;

exultem com tremor.

12Beijem o filho,2.12 Os versículos 11 e 12 permitem traduções alternativas. para que ele não se ire

e vocês não sejam destruídos de repente,

pois num instante acende-se a sua ira.

Como são felizes todos os que nele se refugiam!