Masalimo 19 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 19:1-14

Salimo 19

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu;

thambo limalalikira ntchito za manja ake.

2Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri,

usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.

3Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse;

liwu lawo silimveka.

4Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi,

mawuwo amafika mpaka

kumalekezero a dziko lapansi.

5Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake,

ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.

6Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo

ndi kuzungulira mpaka mbali inanso;

palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.

7Lamulo la Yehova ndi langwiro,

kutsitsimutsa moyo.

Maumboni a Yehova ndi odalirika,

amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.

8Malangizo a Yehova ndi olungama,

amapereka chimwemwe mu mtima.

Malamulo a Yehova ndi onyezimira,

amapereka kuwala.

9Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro,

chimakhala mpaka muyaya.

Maweruzo a Yehova ndi owona

ndipo onse ndi olungama;

10ndi a mtengowapatali kuposa golide,

kuposa golide weniweni;

ndi otsekemera kuposa uchi,

kuposa uchi wochokera pa chisa chake.

11Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo;

powasunga pali mphotho yayikulu.

12Ndani angathe kudziwa zolakwa zake?

Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.

13Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa;

iwo asandilamulire.

Kotero ndidzakhala wosalakwa,

wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.

14Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga

zikhale zokondweretsa pamaso panu,

Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.

Hoffnung für Alle

Psalm 19:1-15

Gottes gute Ordnungen in der Schöpfung und in seinem Gesetz

1Ein Lied von David.

2Der Himmel verkündet Gottes Hoheit und Macht,

das Firmament bezeugt seine großen Schöpfungstaten.

3Ein Tag erzählt dem nächsten davon,

und eine Nacht sagt es der anderen weiter.

4Dies alles geschieht ohne Worte,

ohne einen vernehmlichen Laut.

5Doch auf der ganzen Erde hört man diese Botschaft,

sie erreicht noch die fernsten Länder.

Der Sonne hat Gott am Himmel ein Zelt aufgeschlagen.

6Am Morgen kommt sie strahlend heraus

wie ein Bräutigam aus seiner Kammer.

Siegesgewiss wie ein Held beginnt sie ihren Lauf;

7am fernen Horizont geht sie auf

und wandert von einem Ende des Himmels zum andern.

Nichts bleibt vor ihrer Hitze verborgen.

8Das Gesetz des Herrn ist vollkommen,

es belebt und schenkt neue Kraft.

Auf seine Gebote kann man sich verlassen.

Sie machen auch den klug,

der bisher gedankenlos in den Tag hineinlebte.

9Die Weisungen des Herrn sind zuverlässig

und erfreuen das Herz.

Die Befehle des Herrn sind klar;

Einsicht gewinnt, wer auf sie achtet.

10Die Ehrfurcht vor dem Herrn ist gut, nie wird sie aufhören.

Die Gebote, die der Herr gegeben hat,

sind richtig, vollkommen und gerecht.

11Sie lassen sich nicht mit Gold aufwiegen,

sie sind süßer als der beste Honig.

12Herr, ich will dir dienen.

Wie gut, dass mich dein Gesetz vor falschen Wegen warnt!

Wer sich an deine Gebote hält, wird reich belohnt.

13Wer aber kann erkennen, ob er nicht doch vom rechten Weg abkommt?

Vergib mir die Verfehlungen, die mir selbst nicht bewusst sind!

14Bewahre mich vor mutwilligen Sünden19,14 Oder: vor gewissenlosen Menschen.

und lass nicht zu, dass sie Macht über mich gewinnen;

dann werde ich dir nie mehr die Treue brechen

und frei sein von schwerer Schuld.

15Herr, lass dir meine Worte und Gedanken gefallen!

Du bist mein schützender Fels, mein starker Erlöser!