Masalimo 18 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 18:1-50

Salimo 18

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.

1Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.

2Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga;

Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo.

Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.

3Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando,

ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.

4Zingwe za imfa zinandizinga;

mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.

5Anandimanga ndi zingwe za ku manda;

misampha ya imfa inalimbana nane.

6Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;

ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize.

Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga;

kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.

7Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi,

ndipo maziko a mapiri anagwedezeka;

ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.

8Mʼmphuno mwake munatuluka utsi;

moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake,

makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.

9Iye anangʼamba thambo natsika pansi;

pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.

10Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka;

nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.

11Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake,

chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.

12Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala,

makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.

13Yehova anabangula kumwamba ngati bingu,

mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.

14Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake,

ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.

15Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera;

maziko a dziko lapansi anakhala poyera,

Yehova atabangula mwaukali,

pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.

16Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira;

anandivuwula mʼmadzi ozama.

17Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.

18Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto,

koma Yehova anali thandizo langa.

19Iye anandipititsa kumalo otakasuka;

anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.

20Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa;

molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.

21Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova;

ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.

22Malamulo ake onse ali pamaso panga;

sindinasiye malangizo ake.

23Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake

ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.

24Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa,

molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.

25Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu;

kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,

26kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu,

koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.

27Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa,

koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.

28Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe;

Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.

29Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo;

ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.

30Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro;

mawu a Yehova alibe cholakwika.

Iye ndi chishango

kwa onse amene amathawira kwa Iye.

31Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova?

Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?

32Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu

ndi kulungamitsa njira yanga.

33Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi;

Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.

34Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.

35Inu mumandipatsa chishango chachipambano,

ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza;

mumawerama pansi kundikuza.

36Munakulitsa njira yoyendamo ine,

kuti mapazi anga asaguluke.

37Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira;

sindinabwerere mpaka atawonongedwa.

38Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka;

anagwera pa mapazi anga.

39Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo,

munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.

40Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa,

ndipo ine ndinawononga adani angawo.

41Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa.

Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.

42Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo.

Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.

43Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu;

mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina.

Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.

44Alendo amadzipereka okha pamaso panga;

akangomva za ine amandigonjera.

45Iwo onse anataya mtima;

anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.

46Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa!

Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!

47Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango,

amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,

48amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga.

Inu munandikuza kuposa adani anga;

munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.

49Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova;

ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.

50Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake;

amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake,

kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.

New Serbian Translation

Псалми 18:1-50

Псалам 18

Давид је испевао Господу речи ове песме онога дана када га је Господ избавио из руку свих његових непријатеља и из Саулове руке. Рекао је:

1Волим те, Господе, моја снаго.

2Господе, стено моја,

тврђаво моја, избавитељу мој.

Мој Бог је мени стена,

где заклон налазим.

Штите мој, роже мог спасења,

заклоне мој, уточиште моје!

3Призваћу Господа славе предостојног,

и он ће ме спасти од мојих душмана.

4Смртна су се ужад сплела око мене,

ужаснут сам разорним рекама.

5Ужад су ме Света мртвих опколила,

смрт ме вреба са својим замкама.

6У невољи завапих Господу,

и повиках ка Богу својему.

Из свог храма глас је мој чуо,

мој вапај стиже до њега,

до његових ушију.

7Тад се земља уздрма, затресе,

задрхташе темељи планина,

стресоше се због његовог гнева.

8Дим се диже њему из ноздрва,

огањ пламти из његових уста,

жар угљени из њега избија.

9Он небеса пресави и сиђе,

под ногама густа му је тама.

10Херувима узјаха, полете,

и заплови на крилима ветра.

11Од таме начини око себе шатор,

сеницу за себе од тамних вода

и од облака тамних.

12Од сјаја пред њим прођоше облаци,

пљушти град и угаљ ужарени.

13Тада Господ загрме с небеса,

разлеже се глас Свевишњега,

град и угаљ ужарени.

14Стреле своје одапе и душмане расу,

бљесну муњама, у пометњу их баци.

15Кад си Господе почео да караш,

кад ти дах из ноздрва плану,

долине се водне показаше,

открише се темељи света.

16Руку пружи са висина, дохвати ме,

из вода ме моћних извуче,

17од моћног ме избави душмана,

и од оних јачих што ме мрзе.

18Навалише на мене у дан моје муке,

али Господ ми је био ослонац.

19Изведе ме на пространо место,

избави ме јер сам му по вољи.

20Господ ми по правди мојој плати,

награди ми чистоћу руку мојих,

21јер путеве Господње сачувах;

Богу своме ја нисам скривио.

22Судови његови сви су ми пред очима,

од одредби његових одвратио се нисам.

23Пред њим сам ја био беспрекоран,

сачувао сам себе од кривице,

24по правди ме је мојој Господ наградио,

руке су ми недужне пред његовим очима.

25Ти вернима исказујеш верност,

беспрекорнима узвраћаш поштењем.

26С чистима ти поступаш чисто,

а с опакима поступаш лукаво.

27Ти избављаш кротак народ,

а обараш поглед узносити.

28Јер ти, Господе, светиљку ми палиш,

мој Бог моју таму расветљује.

29Јер са тобом ја разбијам чету,

с Богом мојим прескачем зидине.

30Пут је Божији беспрекоран,

реч је Господња у ватри прекаљена;

штит је свима што у њему уточиште траже.

31Јер ко је Бог осим Господа?

Ко је стена осим нашег Бога?

32Он је Бог који ме снагом опрема,

он пут мој чини беспрекорним.

33Даде ми ноге хитре ко у кошуте,

постави ме чврсто на висине.

34Руке моје учи војевању,

да лук бронзани натежем мишицама.

35Ти ми дајеш штит спасења свога,

десница ме твоја подупире,

твој одазив чини ме великим.

36Шириш тло под кораком мојим,

да ми ноге не би посрнуле.

37Душмане своје гоним и сустижем,

не враћам се док их не докрајчим.

38Разбијам их и не могу устати,

и падају под моје ноге.

39Ти ме опремаш снагом за битку,

и обараш пода мном моје противнике.

40Ти учини да душмани моји

реп свој подвију преда мном,

да мрзитеље своје искореним.

41Завапише, али им спаса нема ниоткуда;

Господу завапише, али он им не одговара.

42Измрвих их као прах пред ветар,

избацих их као блато са улица.

43Ти си ме избавио од сукоба с народом,

и поставио ме за главу пуцима.

Народ који нисам знао,

тај ми народ служи.

44Туђинци ми ласкају,

чим ме чују, они ме слушају.

45Туђинци губе срчаност,

из својих тврђава излазе дрхћући.

46Живео Господ! Благословена била стена моја!

Узвишен био Бог мога спасења!

47То је Бог што ме освећује,

он мени покорава народе;

48избавља ме од мојих душмана.

Над мојим си ме мрзитељима узвисио,

избавио ме од човека насилног.

49Зато ћу те хвалити, Господе, међу пуцима,

твоје ћу име песмом прослављати.

50Велико спасење даје своме цару;

исказује милост помазанику своме, Давиду,

и његовом потомству довека.