Masalimo 15 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 15:1-5

Salimo 15

Salimo la Davide.

1Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?

Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?

2Munthu wa makhalidwe abwino,

amene amachita zolungama,

woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,

3ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,

amene sachitira choyipa mnansi wake

kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,

4amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.

Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,

amene amakwaniritsa zomwe walonjeza

ngakhale pamene zikumupweteka,

5amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja

ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.

Iye amene amachita zinthu zimenezi

sadzagwedezeka konse.

New International Version

Psalms 15:1-5

Psalm 15

A psalm of David.

1Lord, who may dwell in your sacred tent?

Who may live on your holy mountain?

2The one whose walk is blameless,

who does what is righteous,

who speaks the truth from their heart;

3whose tongue utters no slander,

who does no wrong to a neighbor,

and casts no slur on others;

4who despises a vile person

but honors those who fear the Lord;

who keeps an oath even when it hurts,

and does not change their mind;

5who lends money to the poor without interest;

who does not accept a bribe against the innocent.

Whoever does these things

will never be shaken.