Salimo 15
Salimo la Davide.
1Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?
Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
2Munthu wa makhalidwe abwino,
amene amachita zolungama,
woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
3ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,
amene sachitira choyipa mnansi wake
kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
4amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.
Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,
amene amakwaniritsa zomwe walonjeza
ngakhale pamene zikumupweteka,
5amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja
ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.
Iye amene amachita zinthu zimenezi
sadzagwedezeka konse.
Dwom 15
Dawid dwom.
1Awurade, hena na ɔbɛtena wo kronkronbea ntamadan no mu?
Hena na ɔbɛtena wo bepɔw kronkron no so?
2Nea ne ho nni asɛm
na ɔyɛ nea ɛteɛ,
nea ɔka nokware a efi ne koma mu
3na ɔmfa ne tɛkrɛma nsɛe nnipa
nea ɔnyɛ ne yɔnko bɔne
na ommu ne yɔnko nipa abomfiaa,
4nea obu afideyɛni animtiaa
na ɔde nidi ma wɔn a wosuro Awurade,
nea odi ne ntam so,
bere a etia no mpo,
5nea ɔde ne sika bɔ bosea a onnye nsiho
na onnye adanmude ntia nea odi bem.
Nea ɔyɛ eyinom no
renhinhim da.