Masalimo 15 – CCL & AKCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 15:1-5

Salimo 15

Salimo la Davide.

1Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?

Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?

2Munthu wa makhalidwe abwino,

amene amachita zolungama,

woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,

3ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,

amene sachitira choyipa mnansi wake

kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,

4amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.

Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,

amene amakwaniritsa zomwe walonjeza

ngakhale pamene zikumupweteka,

5amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja

ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.

Iye amene amachita zinthu zimenezi

sadzagwedezeka konse.

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 15:1-5

Dwom 15

Dawid dwom.

1Awurade, hena na ɔbɛtena wo kronkronbea ntamadan no mu?

Hena na ɔbɛtena wo bepɔw kronkron no so?

2Nea ne ho nni asɛm

na ɔyɛ nea ɛteɛ,

nea ɔka nokware a efi ne koma mu

3na ɔmfa ne tɛkrɛma nsɛe nnipa

nea ɔnyɛ ne yɔnko bɔne

na ommu ne yɔnko nipa abomfiaa,

4nea obu afideyɛni animtiaa

na ɔde nidi ma wɔn a wosuro Awurade,

nea odi ne ntam so,

bere a etia no mpo,

5nea ɔde ne sika bɔ bosea a onnye nsiho

na onnye adanmude ntia nea odi bem.

Nea ɔyɛ eyinom no

renhinhim da.