Masalimo 148 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 148:1-14

Salimo 148

1Tamandani Yehova.

Tamandani Yehova, inu a kumwamba,

mutamandeni Iye, inu a mlengalenga.

2Mutamandeni, inu angelo ake onse,

mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba.

3Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi,

mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala.

4Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba

ndi inu madzi a pamwamba pa thambo.

5Zonse zitamande dzina la Yehova

pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.

6Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi;

analamula ndipo sizidzatha.

7Tamandani Yehova pa dziko lapansi,

inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,

8inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo,

mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,

9inu mapiri ndi zitunda zonse,

inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,

10inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse,

inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.

11Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse,

inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.

12Inu anyamata ndi anamwali,

inu nkhalamba ndi ana omwe.

13Onsewo atamande dzina la Yehova

pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka;

ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.

14Iye wakwezera nyanga anthu ake,

matamando a anthu ake onse oyera mtima,

Aisraeli, anthu a pamtima pake.

Tamandani Yehova.

New Serbian Translation

Псалми 148:1-14

Псалам 148

1Славите Господа!

Славите Господа са небеса,

славите га на висинама!

2О, анђели сви његови, славите га,

славите га, све војске његове!

3Славите га, сунце и месече,

славите га, све блиставе звезде!

4Славите га, небеса највиша,

и ви, воде врх небеса!

5Нек Господње име славе,

јер он заповеди и они посташе.

6За сву вечност њих је поставио,

уредбу је дао која проћи неће.

7Ви са земље славите Господа –

немани морске и дубино свака;

8громе и граде, снеже и магло,

олујо што реч његову остварујеш;

9горе и сва брда, свако стабло родно

и сви кедрови;

10звери и сва стоко,

гмизавци и птице крилате;

11земаљски цареви и сви људи,

главари и владари земље;

12младићи, а и девојке;

стари са младима!

13Нек Господње име славе,

јер само је његово име узвишено;

величанство му је и над земљом и над небесима!

14Свом народу он ће рог уздићи –

славу сваког који му је веран –

народу израиљском, народу њему блиском.

Славите Господа!