Masalimo 146 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 146:1-10

Salimo 146

1Tamandani Yehova.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

2Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.

3Musamadalire mafumu,

anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.

4Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi;

zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.

5Wodala ndi amene thandizo lake ndi

Mulungu wa Yakobo.

6Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi,

nyanja ndi zonse zili mʼmenemo;

Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.

7Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa

ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala.

Yehova amamasula amʼndende,

8Yehova amatsekula maso anthu osaona,

Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi,

Yehova amakonda anthu olungama.

9Yehova amasamalira alendo

ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye,

koma amasokoneza njira za anthu oyipa.

10Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse.

Tamandani Yehova.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 146:1-10

Om at sætte sin lid til Herren

1Halleluja!

Min sjæl, pris Herren!

2Jeg vil lovprise Herren, så længe jeg lever,

synge til hans ære, så længe jeg trækker vejret.

3Stol ikke på stormænd,

for mennesker kan ikke frelse jer.

4De dør og bliver lagt i deres grav,

da er det slut med alle deres planer.

5Velsignede er de, der stoler på Israels Gud,

de, der sætter deres lid til Herren.

6Han skabte himlen og jorden,

havet og alt, hvad der lever deri.

Han er trofast til evig tid.

7Han står på de undertryktes side

og sørger for mad til de sultne.

Han sætter fanger i frihed

8og åbner de blindes øjne.

Han løfter de nedbrudte op,

han elsker dem, der gør hans vilje.

9Han tager sig af de fremmede,

viser omsorg for enker og forældreløse,

men de ondes planer forpurrer han.

10Herren skal regere for evigt!

Jerusalem, din Gud er konge fra slægt til slægt!

Halleluja!