Masalimo 144 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 144:1-15

Salimo 144

Salimo la Davide.

1Atamandike Yehova Thanthwe langa,

amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

zala zanga kumenya nkhondo.

2Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,

linga langa ndi mpulumutsi wanga,

chishango changa mmene ine ndimathawiramo,

amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

3Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,

mwana wa munthu kuti muzimuganizira?

4Munthu ali ngati mpweya;

masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

5Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;

khudzani mapiri kuti atulutse utsi.

6Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;

ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.

7Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;

landitseni ndi kundipulumutsa,

ku madzi amphamvu,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

8amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

9Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;

ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,

10kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,

amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.

11Landitseni ndi kundipulumutsa,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

12Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo

adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,

ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala

zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.

13Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza

ndi zokolola za mtundu uliwonse.

Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda

pa mabusa athu.

14Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.

Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,

sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,

mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.

15Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;

odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

Swedish Contemporary Bible

Psaltaren 144:1-15

Psalm 144

Glädje över Guds omsorg

1Av David.

Lovad vare Herren, min klippa,

han som lär mina händer att kriga

och mina fingrar att strida,

2han som är nådig mot mig,

min klippa, min borg,

min befriare och min sköld.

Hos honom söker jag tillflykt.

Han har lagt mitt folk under mig.

3Herre, vad är en människa, att du bryr dig om henne,

ett människobarn för din omtanke?

4Människan är som en vindfläkt,

hennes liv som en flyende skugga.

5Herre, dra undan himlen och stig ner!

Rör vid bergen, så att de ryker.

6Släpp loss blixtarna och skingra dem,

skjut iväg pilarna och driv bort dem.

7Sträck ner dina händer från höjden,

rädda mig, befria mig ur de djupa vattnen,

ur främlingarnas våld.

8Deras mun är full av lögn

och deras högra hand av bedrägeri.

9För dig, Gud, vill jag sjunga en ny sång

och spela på en tiosträngad harpa,

10för du räddar kungarna från nederlaget

och befriar din tjänare David från det onda svärdet.

11Rädda mig! Befria mig från främlingarnas våld!

De, vars munnar är fulla av lögner

och vilkas högra hand är redo till bedrägeri.

12Våra unga söner blir som välväxta plantor,

våra döttrar som pelare, uthuggna för palats.

13Våra lador blir fyllda till brädden

av livets förnödenheter av alla slag.

Ute på våra marker får fåren tusentals,

ja, tiotusentals med lamm,

14och oxarna är tungt lastade med spannmål.

I muren finns inte längre någon rämna,

ingen fördrivs,

på våra gator finns inte längre någon som klagar.

15Lyckligt är det folk som har det så.

Ja, lyckligt är det folk vars Gud är Herren!