Masalimo 144 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 144:1-15

Salimo 144

Salimo la Davide.

1Atamandike Yehova Thanthwe langa,

amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

zala zanga kumenya nkhondo.

2Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,

linga langa ndi mpulumutsi wanga,

chishango changa mmene ine ndimathawiramo,

amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

3Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,

mwana wa munthu kuti muzimuganizira?

4Munthu ali ngati mpweya;

masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

5Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;

khudzani mapiri kuti atulutse utsi.

6Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;

ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.

7Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;

landitseni ndi kundipulumutsa,

ku madzi amphamvu,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

8amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

9Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;

ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,

10kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,

amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.

11Landitseni ndi kundipulumutsa,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

12Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo

adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,

ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala

zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.

13Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza

ndi zokolola za mtundu uliwonse.

Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda

pa mabusa athu.

14Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.

Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,

sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,

mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.

15Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;

odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

New International Version

Psalms 144:1-15

Psalm 144

Of David.

1Praise be to the Lord my Rock,

who trains my hands for war,

my fingers for battle.

2He is my loving God and my fortress,

my stronghold and my deliverer,

my shield, in whom I take refuge,

who subdues peoples144:2 Many manuscripts of the Masoretic Text, Dead Sea Scrolls, Aquila, Jerome and Syriac; most manuscripts of the Masoretic Text subdues my people under me.

3Lord, what are human beings that you care for them,

mere mortals that you think of them?

4They are like a breath;

their days are like a fleeting shadow.

5Part your heavens, Lord, and come down;

touch the mountains, so that they smoke.

6Send forth lightning and scatter the enemy;

shoot your arrows and rout them.

7Reach down your hand from on high;

deliver me and rescue me

from the mighty waters,

from the hands of foreigners

8whose mouths are full of lies,

whose right hands are deceitful.

9I will sing a new song to you, my God;

on the ten-stringed lyre I will make music to you,

10to the One who gives victory to kings,

who delivers his servant David.

From the deadly sword 11deliver me;

rescue me from the hands of foreigners

whose mouths are full of lies,

whose right hands are deceitful.

12Then our sons in their youth

will be like well-nurtured plants,

and our daughters will be like pillars

carved to adorn a palace.

13Our barns will be filled

with every kind of provision.

Our sheep will increase by thousands,

by tens of thousands in our fields;

14our oxen will draw heavy loads.144:14 Or our chieftains will be firmly established

There will be no breaching of walls,

no going into captivity,

no cry of distress in our streets.

15Blessed is the people of whom this is true;

blessed is the people whose God is the Lord.