Masalimo 143 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 143:1-12

Salimo 143

Salimo la Davide.

1Yehova imvani pemphero langa,

mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;

mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu

bwerani kudzandithandiza.

2Musazenge mlandu mtumiki wanu,

pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

3Mdani akundithamangitsa,

iye wandipondereza pansi;

wachititsa kuti ndikhale mu mdima

ngati munthu amene anafa kale.

4Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;

mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

5Ndimakumbukira masiku amakedzana;

ndimalingalira za ntchito yanu yonse,

ndimaganizira zimene manja anu anachita.

6Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.

Sela

7Yehova ndiyankheni msanga;

mzimu wanga ukufowoka.

Musandibisire nkhope yanu,

mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

8Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,

pakuti ine ndimadalira Inu.

Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,

pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.

9Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,

pakuti ndimabisala mwa Inu.

10Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,

popeza ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu wabwino unditsogolere

pa njira yanu yosalala.

11Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.

12Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;

wonongani adani anga,

pakuti ndine mtumiki wanu.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 143:1-12

Bøn om befrielse

1En sang af David.

Herre, hør min bøn!

Lyt til mit indtrængende råb!

Svar mig, for du er trofast og god.

2Fordøm mig ikke, Herre,

for ingen er fejlfri i dine øjne.

3Mine fjender forfølger mig,

de har spoleret mit liv.

De tvinger mig til at leve i mørket,

som om jeg allerede var død.

4Modet svigter mig,

jeg er lammet af frygt.

5Jeg tænker på gamle dage,

jeg mindes dine mægtige undere,

jeg husker det, du gjorde engang.

6Jeg rækker ud efter dig med længsel,

min sjæl tørster som den tørre jord.

7Skynd dig at hjælpe mig, Herre,

for jeg kan snart ikke mere.

Vend mig ikke ryggen,

for så er det ude med mig.

8Lad mig smage din godhed hver morgen,

for det er dig, jeg sætter min lid til.

Vis mig din vilje med mit liv,

for det er dig, jeg ønsker at følge.

9Frels mig fra mine fjender, Herre,

for det er hos dig, jeg har søgt tilflugt.

10Lær mig at gøre din vilje,

for det er dig, der er min Gud.

Led mig ved din gode Ånd

til et sted, hvor jeg kan leve i fred.

11Frels mig, Herre, for din æres skyld,

hjælp mig for din godheds skyld.

12Uskadeliggør alle mine fjender,

for jeg er din tjener.