Masalimo 141 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 141:1-10

Salimo 141

Salimo la Davide.

1Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.

Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.

2Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;

kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

3Yehova ikani mlonda pakamwa panga;

londerani khomo la pa milomo yanga.

4Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;

kuchita ntchito zonyansa

pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;

musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.

5Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;

andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.

Mutu wanga sudzakana zimenezi.

Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.

6Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,

ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.

7Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,

ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”

8Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;

ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.

9Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,

ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.

10Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,

mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

O Livro

Salmos 141:1-10

Salmo 141

Salmo de David.

1Senhor, rogo-te,

ouve a minha oração, escuta-me!

2Recebe a minha oração,

como o fumo do incenso que sobe na tua presença,

e o levantar das minhas mãos

como um dos sacrifícios da tarde.

3Põe, ó Senhor, uma guarda à minha boca,

uma sentinela aos meus lábios.

4Não deixes que o meu coração se incline para o mal,

que se ocupe de coisas más,

que se junte com os que praticam a maldade,

participando nos seus gozos e excessos.

5Se tiver de ser castigado,

que seja por pessoas justas.

Se esses me repreenderem,

até isso considerarei como um benefício

que não deixarei de aceitar.

Quanto à gente perversa,

continuarei a orar contra as maldades deles!

6Os juízes deles ouvirão as minhas palavras

e saberão que são bem intencionadas.

7Assim como se sulca e lavra a terra,

assim também os nossos ossos são espalhados

ao abrir-se o mundo dos mortos.

8Mas eu espero a tua ajuda, Senhor, meu Deus;

confio em ti, não me desampares.

9Guarda-me das ciladas que me armam,

das ratoeiras que põem no meu caminho,

essa gente que pratica a iniquidade.

10Sejam eles a cair nas armadilhas que preparam

e que eu fique inteiramente livre deles!