Masalimo 140 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 140:1-13

Salimo 140

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Landitseni Yehova kwa anthu oyipa;

tetezeni kwa anthu ankhanza,

2amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa

ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.

3Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka;

pa milomo yawo pali ululu wa mamba.

Sela

4Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa;

tchinjirizeni kwa anthu ankhanza

amene amakonza zokola mapazi anga.

5Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika;

iwo atchera zingwe za maukonde awo

ndipo anditchera misampha pa njira yanga.

Sela

6Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

Imvani kupempha kwanga Yehova.

7Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu,

mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.

8Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova;

musalole kuti zokonza zawo zitheke,

mwina iwo adzayamba kunyada.

Sela

9Mitu ya amene andizungulira

iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.

10Makala amoto agwere pa iwo;

aponyedwe pa moto,

mʼmaenje amatope, asatulukemonso.

11Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko;

choyipa chilondole anthu ankhanza.

12Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka,

ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.

13Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu,

ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 140:1-13

Salmo 140

Al director musical. Salmo de David.

1Oh Señor, líbrame de los impíos;

protégeme de los violentos,

2de los que urden en su corazón planes malvados

y todos los días fomentan la guerra.

3Afilan su lengua cual lengua de serpiente;

¡veneno de víbora hay en sus labios! Selah

4Señor, protégeme del poder de los impíos;

protégeme de los violentos,

de los que piensan hacerme caer.

5Esos engreídos me han tendido una trampa;

han puesto los lazos de su red,

han tendido trampas a mi paso. Selah

6Yo le digo al Señor: «Tú eres mi Dios.

Atiende, Señor, a mi voz suplicante».

7Señor Soberano, mi Salvador poderoso

que me protege en el día de la batalla:

8No satisfagas, Señor, los caprichos de los impíos;

no permitas que sus planes prosperen,

para que no se enorgullezcan. Selah

9Que sobre la cabeza de mis perseguidores

recaiga el mal que sus labios proclaman.

10Que lluevan brasas sobre ellos;

que sean echados en el fuego,

en ciénagas profundas, de donde no vuelvan a salir.

11Que no eche raíces en la tierra

la gente de lengua viperina;

que la calamidad persiga y destruya

a la gente que practica la violencia.

12Yo sé que el Señor hace justicia a los pobres

y defiende el derecho de los necesitados.

13Ciertamente los justos alabarán tu nombre

y los íntegros vivirán en tu presencia.