Salimo 138
Salimo la Davide.
1Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse;
ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
2Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera
ndipo ndidzayamika dzina lanu
chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu,
pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu
kupambana zinthu zonse.
3Pamene ndinayitana, munandiyankha;
munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
4Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova,
pamene amva mawu a pakamwa panu.
5Iwo ayimbe za njira za Yehova,
pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
6Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa,
koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
7Ngakhale ndiyende pakati pa masautso,
mumasunga moyo wanga;
mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga,
mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
8Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine;
chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha
musasiye ntchito ya manja anu.
Salmo 138
Salmo de David.
1Señor, quiero alabarte de todo corazón,
y cantarte salmos delante de los dioses.
2Quiero inclinarme hacia tu santo templo
y alabar tu nombre por tu gran amor y fidelidad.
Porque has exaltado tu nombre y tu palabra
por encima de todas las cosas.
3Cuando te llamé, me respondiste;
me infundiste ánimo y renovaste mis fuerzas.
4Oh Señor, todos los reyes de la tierra
te alabarán al escuchar tus palabras.
5Celebrarán con cánticos tus caminos,
porque tu gloria, Señor, es grande.
6El Señor es excelso,
pero tiene en cuenta a los humildes
y mira138:6 mira. Lit. conoce. de lejos a los orgullosos.
7Aunque pase yo por grandes angustias,
tú me darás vida;
contra el furor de mis enemigos extenderás la mano:
¡tu mano derecha me pondrá a salvo!
8El Señor cumplirá en mí su propósito.138:8 El Señor … su propósito. Lit. El Señor completará en mí.
Tu gran amor, Señor, perdura para siempre;
¡no abandones la obra de tus manos!