Salimo 137
1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira
pamene tinakumbukira Ziyoni.
2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi
tinapachika apangwe athu,
3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.
Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;
iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova
mʼdziko lachilendo?
5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,
dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga
ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,
ngati sindiyesa iwe
chimwemwe changa chachikulu.
7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita
pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.
Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi
mpaka pa maziko ake!”
8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,
wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera
pa zimene watichitira.
9Amene adzagwira makanda ako
ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
1Wij zaten aan de rivier in de stad Babel
en huilden toen wij aan Jeruzalem dachten.
2Onze citers hadden wij daar
aan de takken van een wilg gehangen,
3omdat onze bewakers wilden dat wij zouden zingen.
Ondanks dat zij ons sloegen,
wilden zij een vrolijk lied horen.
‘Vooruit,’ zeiden zij, ‘zing eens een lied over Jeruzalem!’
4Maar hoe kunnen wij nu in een vreemd land
een lied voor de Here zingen?
5Mijn rechterhand mag verlamd raken,
als ik Jeruzalem zou vergeten!
6Als ik Jeruzalem niet zou bezingen
als de mooiste en hoogste stad,
zou mijn tong krachteloos
in mijn mond mogen liggen.
7Neem wraak, Here, op de Edomieten
die Jeruzalem hebben verwoest.
Zij zeiden tegen elkaar:
‘Wij breken die stad tot op de bodem af!’
8Volk van Babel, binnenkort
zal uw eigen land worden verwoest.
Wij prijzen hen die vergelding zullen uitoefenen
over wat u ons hebt aangedaan.
9Wij prijzen degene die nu
úw kinderen tegen de rotsen te pletter zal gooien.