Masalimo 137 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 137:1-9

Salimo 137

1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira

pamene tinakumbukira Ziyoni.

2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi

tinapachika apangwe athu,

3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.

Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;

iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova

mʼdziko lachilendo?

5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,

dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.

6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga

ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,

ngati sindiyesa iwe

chimwemwe changa chachikulu.

7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita

pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.

Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi

mpaka pa maziko ake!”

8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,

wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera

pa zimene watichitira.

9Amene adzagwira makanda ako

ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

Het Boek

Psalmen 137:1-9

1Wij zaten aan de rivier in de stad Babel

en huilden toen wij aan Jeruzalem dachten.

2Onze citers hadden wij daar

aan de takken van een wilg gehangen,

3omdat onze bewakers wilden dat wij zouden zingen.

Ondanks dat zij ons sloegen,

wilden zij een vrolijk lied horen.

‘Vooruit,’ zeiden zij, ‘zing eens een lied over Jeruzalem!’

4Maar hoe kunnen wij nu in een vreemd land

een lied voor de Here zingen?

5Mijn rechterhand mag verlamd raken,

als ik Jeruzalem zou vergeten!

6Als ik Jeruzalem niet zou bezingen

als de mooiste en hoogste stad,

zou mijn tong krachteloos

in mijn mond mogen liggen.

7Neem wraak, Here, op de Edomieten

die Jeruzalem hebben verwoest.

Zij zeiden tegen elkaar:

‘Wij breken die stad tot op de bodem af!’

8Volk van Babel, binnenkort

zal uw eigen land worden verwoest.

Wij prijzen hen die vergelding zullen uitoefenen

over wat u ons hebt aangedaan.

9Wij prijzen degene die nu

úw kinderen tegen de rotsen te pletter zal gooien.