Masalimo 135 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 135:1-21

Salimo 135

1Tamandani Yehova.

Tamandani dzina la Yehova;

mutamandeni, inu atumiki a Yehova,

2amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova,

mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

3Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino;

imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,

4Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake,

Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.

5Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu,

kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.

6Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera,

kumwamba ndi dziko lapansi,

ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.

7Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi,

amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula

ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.

8Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,

ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.

9Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto,

kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.

10Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu

ndi kupha mafumu amphamvu:

11Sihoni mfumu ya Aamori,

Ogi mfumu ya Basani,

ndi maufumu onse a ku Kanaani;

12ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa,

cholowa cha anthu ake Aisraeli.

13Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya,

mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.

14Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa,

ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.

15Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide,

opangidwa ndi manja a anthu.

16Pakamwa ali napo koma sayankhula

maso ali nawo, koma sapenya;

17makutu ali nawo, koma sakumva

ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.

18Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo,

chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.

19Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova;

inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;

20Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova;

Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.

21Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni,

amene amakhala mu Yerusalemu.

Tamandani Yehova.

Hoffnung für Alle

Psalm 135:1-21

Der Herr ist mächtiger als alle Götter!

1Halleluja – lobt den Herrn!

Preist den Namen des Herrn,

ja, lobt ihn, alle seine Diener,

2die ihr in seinem Tempel steht,

in den Vorhöfen beim Haus unseres Gottes!

3Preist den Herrn, denn er ist gut;

musiziert zur Ehre seines herrlichen Namens.

4Er hat die Nachkommen Jakobs auserwählt

und ganz Israel zu seinem Eigentum erklärt.

5Ja, ich habe erkannt: Groß ist der Herr!

Unser Herr ist mächtiger als alle Götter.

6Was er will, das tut er auch –

sei es im Himmel oder auf der Erde,

im Meer oder in den tiefsten Tiefen.

7Er lässt Wolken am Horizont aufsteigen,

er sendet Regen und grelle Blitze,

den Sturmwind holt er aus seiner Kammer

und schickt ihn auf die Reise.

8In Ägypten tötete er alle ältesten Söhne,

die Erstgeborenen von Mensch und Vieh.

9Er vollbrachte dort Zeichen und Wunder

am Pharao und allen seinen Untergebenen.

10Er besiegte viele Völker

und ließ mächtige Könige umkommen:

11Sihon, den König der Amoriter, Og, den König von Baschan,

und alle Könige von Kanaan.

12Die Länder, über die sie geherrscht hatten, übergab er Israel,

sein Volk bekam das ganze Gebiet als bleibenden Besitz.

13Herr, dein Name wird nie in Vergessenheit geraten;

dich wird man rühmen, solange es Menschen gibt.

14Du, Herr, wirst deinem Volk zum Recht verhelfen.

Du erbarmst dich über alle, die dir dienen.

15Die Götter der anderen Völker

sind nur Figuren aus Silber und Gold,

von Menschenhänden gemacht.

16Sie haben einen Mund, aber reden können sie nicht;

Augen haben sie, doch sie können nicht sehen.

17Mit ihren Ohren hören sie nicht,

auch können sie nicht atmen.

18Genauso starr und tot sollen die werden, die diese Götzen schufen,

und auch alle, die solchen Götzen vertrauen!

19Ihr Israeliten, lobt den Herrn!

Ihr Priester,135,19 Wörtlich: Haus Aaron. lobt den Herrn!

20Ihr Leviten, lobt den Herrn!

Alle, die ihr den Herrn achtet – lobt ihn!

21Gelobt sei der Herr auf dem Berg Zion,

denn dort in Jerusalem ist seine Wohnung.

Lobt den Herrn – halleluja!