Masalimo 132 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 132:1-18

Salimo 132

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Inu Yehova, kumbukirani Davide

ndi mavuto onse anapirira.

2Iye analumbira kwa Yehova

ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,

3“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga

kapena kugona pa bedi langa:

4sindidzalola kuti maso anga agone,

kapena zikope zanga ziwodzere,

5mpaka nditamupezera malo Yehova,

malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

6Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,

tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:

7“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;

tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.

8‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,

Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.

9Ansembe anu avekedwe chilungamo;

anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

10Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,

musakane wodzozedwa wanu.

11Yehova analumbira kwa Davide,

lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:

“Mmodzi wa ana ako

ndidzamuyika pa mpando waufumu;

12ngati ana ako azisunga pangano langa

ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,

pamenepo ana awo adzakhala pa mpando

wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

13Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,

Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:

14“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;

ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.

15Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;

anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.

16Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,

ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

17“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide

ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.

18Ndidzaveka adani ake manyazi,

koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

Korean Living Bible

시편 132:1-18

다윗과 여호와의 성전

(성전에 올라가는 노래)

1여호와여,

다윗과 그가 당한

모든 시련을 기억하소서.

2여호와여, 그가 한

약속을 기억하소서.

그가 야곱의 전능하신 하나님께

이런 서약을 하였습니다.

3“내가 내 집이나 침실에

들어가지 않을 것이며

4졸거나 잠을 자지 않을 것이니

5여호와의 성소,

곧 야곱의 전능하신 하나님이

계실 집을 마련하기까지

하리라.”

6우리가 132:6 또는 ‘에브라다’베들레헴에서

법궤에 대한 말을 들었고

그것을 기럇-여아림의

밭에서 찾았다.

7여호와의 집으로 가서

그 앞에 경배하자.

8여호와여, 일어나셔서

주의 능력의 상징인 법궤와 함께

132:8 또는 ‘평안한 곳으로’주의 성소로 들어가소서.

9주의 제사장들은 의의 옷을 입고

주의 성도들은

기쁨으로 노래하게 하소서.

10주의 종 다윗을 생각해서라도

주께서 기름 부어 세운 왕을

물리치지 마소서.

11주께서 다윗에게

엄숙하게 약속하셨으니

이 약속을

취소하지 못하실 것입니다.

“나는 네 아들 중 하나를

네 왕위에 앉히리라.

12만일 네 아들들이 내 계약과

내가 그들에게 가르치는

법을 지키면

그들의 자손들도 계속

너를 이어

왕위에 앉을 것이다.”

13여호와께서 시온을 택하시고

그 곳을 자기 거처로

삼고자 말씀하셨다.

14“이 곳은 내가 영원히 쉴 곳이니

내가 여기 머물 것은

이것을 원하였음이라.

15내가 이 성이 필요로 하는 것을

풍족하게 공급해 주고

가난한 자들을

양식으로 만족하게 하리라.

16내가 그 제사장들에게

구원의 옷을 입힐 것이니

그 성도들이 기쁨으로 노래하리라.

17내가 132:17 또는 ‘다윗에게 뿔이 나게 할 것이라’다윗의 후손 가운데 하나를

위대한 왕이 되게 할 것이니

내가 기름 부은 자를 위해

등을 예비하리라.

18내가 그의 원수들에게는

수치로 옷을 입히고

그에게는 면류관을 씌워

빛나게 하리라.”