Masalimo 13 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 13:1-6

Salimo 13

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale?

Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?

2Ndidzalimbana ndi maganizo anga

ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti?

Mpaka liti adani anga adzandipambana?

3Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga.

Walitsani maso anga kuti ndingafe;

4mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,”

ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.

5Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika;

mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.

6Ine ndidzayimbira Yehova

pakuti wandichitira zokoma.

New Serbian Translation

Псалми 13:1-6

Псалам 13

Хоровођи. Псалам Давидов.

1Докле више, докле, о, Господе?

Зар ћеш ме ти ваздан заборављати?

Докле ћеш од мене своје лице крити?

2Докле више да се питам у души,

и сваки дан у срцу тугујем?

Докле ће душманин да буде нада мном?

3Погледај, услиши ме, Господе,

Боже мој, очи ми просветли,

да у сан смртни ја не утонем,

4да не каже непријатељ:

„Ја сам га надјачао“,

и противници не ликују нада мном.

5А ја ћу се у твоју милост уздати,

твоме се спасењу у срцу радовати.

6Певаћу Господу, јер ми је био добростив.