Masalimo 13 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 13:1-6

Salimo 13

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mpaka liti Yehova? Kodi mudzandiyiwala mpaka kalekale?

Mpaka liti mudzandibisira nkhope yanu?

2Ndidzalimbana ndi maganizo anga

ndi kukhala ndi chisoni mu mtima mwanga tsiku lililonse mpaka liti?

Mpaka liti adani anga adzandipambana?

3Ndiyangʼaneni ndi kundiyankha, Inu Yehova Mulungu wanga.

Walitsani maso anga kuti ndingafe;

4mdani wanga adzati, “Ndamugonjetsa,”

ndipo adani anga adzakondwera pamene ine ndagwa.

5Koma ndikudalira chikondi chanu chosasinthika;

mtima wanga umakondwera ndi chipulumutso chanu.

6Ine ndidzayimbira Yehova

pakuti wandichitira zokoma.

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom 13:1-6

Dwom 13

Dawid dwom.

1Ao, Awurade, ɛnkɔsi da bɛn? Wo werɛ bɛfiri me afebɔɔ anaa?

Ɛnkɔsi da bɛn na wode wʼanim bɛhinta me?

2Ɛnkɔsi da bɛn na mene mʼadwendwene bɛdi apereapereɛ

na awerɛhoɔ ahyɛ mʼakoma mu daa?

Mʼatamfoɔ nni me so nkonim nkɔsi da bɛn?

3Te wʼani hwɛ me na bua me, Ao, Awurade, me Onyankopɔn.

Ma mʼani so nyɛ hann, na manna owuo nna.

4Me ɔtamfoɔ bɛka sɛ, “Madi ne so nkonim.”

Na mʼahohiahiafoɔ bɛdi ahurisie ɛberɛ a mahwe ase.

5Nanso mede me ho to wo dɔ a ɛnsa da no so;

mʼakoma di ahurisie wɔ wo nkwagyeɛ mu.

6Mɛto dwom ama Awurade,

ɛfiri sɛ ɔne me adi no yie.