Masalimo 129 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 129:1-8

Salimo 129

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”

anene tsono Israeli;

2“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,

koma sanandipambane.

3Anthu otipula analima pa msana panga

ndipo anapangapo mizere yayitali:

4Koma Yehova ndi wolungama;

Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”

5Onse amene amadana ndi Ziyoni

abwezedwe pambuyo mwamanyazi.

6Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,

umene umafota usanakule;

7sungadzaze manja a owumweta

kapena manja a omanga mitolo.

8Odutsa pafupi asanene kuti,

“Dalitso la Yehova lili pa inu;

tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 129:1-8

第 129 篇

求上帝擊退仇敵

上聖殿朝聖之詩。

1以色列要說:

我從小就深受仇敵的迫害,

2我從小就深受仇敵的迫害,

但他們沒能勝過我。

3他們鞭打我的背,

傷痕如同農夫耕出的長長犁溝。

4耶和華是公義的,

祂砍斷了惡人捆綁我的繩索。

5願所有憎惡錫安的人狼狽而逃。

6願他們像房頂的草,

沒長起來就已枯萎,

7割下來不滿一把,

紮起來不足一捆。

8沒有一個路過的人說:

「願耶和華賜福給你們!

我們奉耶和華的名祝福你們。」