Masalimo 129 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 129:1-8

Salimo 129

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”

anene tsono Israeli;

2“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,

koma sanandipambane.

3Anthu otipula analima pa msana panga

ndipo anapangapo mizere yayitali:

4Koma Yehova ndi wolungama;

Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”

5Onse amene amadana ndi Ziyoni

abwezedwe pambuyo mwamanyazi.

6Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,

umene umafota usanakule;

7sungadzaze manja a owumweta

kapena manja a omanga mitolo.

8Odutsa pafupi asanene kuti,

“Dalitso la Yehova lili pa inu;

tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

Священное Писание

Забур 129:1-8

Песнь 129

Песнь восхождения.

1Из глубин взываю я к Тебе, Вечный.

2Владыка, услышь мой голос;

будь внимателен к моим молениям!

3Если бы Ты, Вечный, вёл счёт беззакониям,

то, о Владыка, кто бы устоял?

4Но у Тебя есть прощение;

пусть боятся Тебя.

5На Вечного я надеюсь, надеется душа моя,

и на слово Его уповаю.

6Душа моя ждёт Владыку

более, чем стражи – утра,

да, более, чем стражи – утра.

7Да уповает Исраил на Вечного,

потому что у Вечного – милость,

и великое избавление – у Него.

8Он избавит Исраил

от всех его беззаконий129:8 См. Мат. 1:21..