Salimo 128
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1Odala ndi onse amene amaopa Yehova,
amene amayenda mʼnjira zake.
2Udzadya chipatso cha ntchito yako;
madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka
mʼkati mwa nyumba yako;
ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi
kuzungulira tebulo lako.
4Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa
amene amaopa Yehova.
5Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni
masiku onse a moyo wako;
uwone zokoma za Yerusalemu,
6ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.
Mtendere ukhale ndi Israeli.
Salmo 128
Cántico de los peregrinos.
1Dichosos todos los que temen al Señor,
los que van por sus caminos.
2Lo que ganes con tus manos, eso comerás;
gozarás de dicha y prosperidad.
3En el seno de tu hogar,
tu esposa será como vid llena de uvas;
alrededor de tu mesa,
tus hijos serán como vástagos de olivo.
4Tales son las bendiciones
de los que temen al Señor.
5Que el Señor te bendiga desde Sión,
y veas la prosperidad de Jerusalén
todos los días de tu vida.
6Que vivas para ver a los hijos de tus hijos.
¡Que haya paz en Israel!