Masalimo 128 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 128:1-6

Salimo 128

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Odala ndi onse amene amaopa Yehova,

amene amayenda mʼnjira zake.

2Udzadya chipatso cha ntchito yako;

madalitso ndi chuma zidzakhala zako.

3Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka

mʼkati mwa nyumba yako;

ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi

kuzungulira tebulo lako.

4Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa

amene amaopa Yehova.

5Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni

masiku onse a moyo wako;

uwone zokoma za Yerusalemu,

6ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israeli.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 128:1-6

Salmo 128

Cántico de los peregrinos.

1Dichosos todos los que temen al Señor,

los que van por sus caminos.

2Lo que ganes con tus manos, eso comerás;

gozarás de dicha y prosperidad.

3En el seno de tu hogar,

tu esposa será como vid llena de uvas;

alrededor de tu mesa,

tus hijos serán como vástagos de olivo.

4Tales son las bendiciones

de los que temen al Señor.

5Que el Señor te bendiga desde Sión,

y veas la prosperidad de Jerusalén

todos los días de tu vida.

6Que vivas para ver a los hijos de tus hijos.

¡Que haya paz en Israel!